Eli Njuchi walengeza kuti sakwanitsa kuyimba nawo pamapwando awiri azamayimbidwe omwe akhale akuchitika m'boma la Salima lero pa 1 March komanso mawa pa 2 March munzinda wa Blantyre kaamba kakuti sakupeza bwino. Katswiriyu wanena izi… ...
Articles By Ben Bongololo
Munthu m'modzi wafa pamene ena 6,145 manja ali ku nkhongo pamene akusowa pokhala kutsatira kusefukira kwa madzi komwe kwa chitika ku Dwangwa m'boma la Nkhotakota. Malingana ndi lipoti lomwe lachokera ku khosolo ya bomali kudzera… ...
"Mwayamba za ndale?" Anthu angoti kukamwa pululu pamene Dr Namadingo amene amadziwikanso bwino ndi dzina loti Doc walengeza kuti “2030 boma” ndipo anthu akhale tcheru. Izi zadzetsa mafunso ochuluka kwa anthu amene amamutsatira bwino. Namadingo… ...
Mayendedwe akhala ovutirapo pamene mlatho wapamtsinje wa Chitete omwe uli pafupi ndi sukulu ya sekondale yoyendera ya Boma Community Day Secondary school (C.D.S.S) mumanisipalite ya Kasungu wakokoloka ndi madzi kutsatira mvula yamphamvu yomwe yagwa kuyambira… ...
M'modzi mwa akatswiri pa nkhani za ulimi a Leonard Chimwanza, wati zotsatira zomwe unduna wa za ulimi watulutsa ponena kuti dziko lino likolola chakudya chochuluka ndizodzetsa mafunso kutengera ndi momwe mbewu ziliri m'minda yambiri mdziko… ...
Njonda ina yazaka 30 zakubadwa m'boma la Mangochi yatsikira kulichete itamira panthawi yomwe iyo imafuna kuba nsomba mumisampha ya asodzi amzake pa doko lina mnyanja ya Malombe. Nkhani yonse ikuti mkuluyu yemwe dzina lake ndi… ...
Bambo wina ku Dowa yemwe dzina lake ndi Kelvin Songazaudzu wa zaka 47 zakubadwa wadzimangilira kudenga la nyumba yake kaamba kamavuto a m'banja. Mneneri wa apolisi m'bomali a MacPatson Msadala watsimikiza za nkhaniyi ndipo wati… ...
Bambo wina wazaka 41 zakubadwa m unzinda wa Lilongwe ku Nsungwi, ali mu ululu mkazi wake atamuthira madzi otentha pamimba ndipo pakadali pano mkaziyu akusungidwa mchitokosi cha apolisi kaamba kochita zaupanduzi. Mkaziyu yemwe dzina lake… ...
M'modzi mwa akatswiri pandale m'dziko muno a Lyford Chadza, wati mtsogoleri wakale wa dziko lino a Peter Mutharika akuyenera kusamala pamene mtsogoleriyu wati ali ndi mau opita kwa mtsogoleri wa dziko a Lazarus Chakwera. Katswiriyu… ...
Nyamata wazaka 19 ku Chilipa m'boma la Mangochi ali m'manja mwa apolisi kaamba koti akuganizilidwa kuti wapha mzake chifukwa cholimbirana mkazi. Woganiziridwayu yemwe dzina lake ndi Anusa Sausande adabaya ndikupha Kassim wazaka 21 zakubadwa pomwe… ...
Nthambi yowona zanyengo ndi kusintha kwa nyengo m'dziko muno ya Department of Climate Change and Meteorological Services (DCCMS) yati kumwamba kudakali madzi amvula ochuluka kotero mvula yamabingu ikhala ikugwa m'madera ochuluka mdziko muno kufikira lachiwiri.… ...
Kuwonjezera kwa ndalama zachitukuko za Constituency Development Fund (CDF) kuchoka pa 100 miliyoni kufika pa 200 million kwacha kunadzetsa chimwemwe chochuluka kwa aphungu ambili pamene nduna ya za chuma a Simplex Chithyola Banda anawuza nyumba… ...
Bambo wazaka 50 a Chiyipila Nsato, ali m'manja mwa apolisi ku Lilongwe kaamba kowaganizira kuti iwo ndi anthu ena atatu anakaba nawo katundu okwana 90 miliyoni kwacha ku likulu la tsopano la Radio Maria. Mneneri… ...
Njonda ina yazaka 30 zakubadwa, yapulumukira mkamwa mwa njovu pamene bwalo lamilandu ku Kasungu lamupeza osalakwa pa mlandu omwe amamuzenga ogonana ndi mtsikana yemwe amati ndi wa zaka 16. Mkuluyu yemwe dzina lake ndi Lameck… ...
Apolisi ya Nkhunga m'boma la Nkhotakota, akusakasaka dalayivala wina yemwe ananyamula chamba cha nkhaninkhani mu galimoto yomwe iye amayendetsa ndipo atazindikira kuti apolisi akumutsatira anayimika galimotoyo pa malo ena mkuliyatsa liwiro la mtondo odooka. Nkhani… ...