Loya wanjatidwa kamba kogula galimoto yobedwa ku South Africa

Advertisement

Katswiri pa nkhani za malamulo a Stanley Chirwa omwe amayimilira anthu pa milandu, ali m’manja mwa apolisi powaganizira kuti anagula galimoto yomwe inabedwa m’dziko la South Africa ndi zigawenga zokhala ndi mfuti.

Ofalitsa nkhani za a Polisi m’dziko muno, a Peter Kalaya, ndi omwe atsimikiza za nkhaniyi ponena kuti a Chirwa amangidwa kumapeto kwa sabata yatha pomwe akuganizilidwa kuti anagula galimoto ya mtundu wa Ford Ranger.

A Kalaya awauza nyumba zina zofalitsa nkhani m’dziko muno kuti galimotoyi idabedwa ndi zigawenga za mfuti m’dziko la South Africa, m’chaka cha 2018.

Apolisiwa ati nkhaniyi yadziwika pomwe pa 8 April chaka chino, a Chirwa anapita ndi galimotoyi ku Road Traffic kuti akayilembetse ndipo uku nkomwe akuti anaizindikira kuti galimotoyi ikufanana ndi ina yomwe idabedwa ndi zigawenga m’dziko la South Africa.

Apa a Polisi anamufunsa katswiri wa za malamuloyu za komwe anatenga galimotoyi ndipo iye anasankha kusalankhura kanthu zomwe zapangitsa kuti a Polisi akhazikitse kafukufuku pa nkhaniyi yemwe anakali mkati.

Pakadali pano a Chirwa sanaonekerebe ku bwalo la milandu kuti awauze milandu yomwe akuzengedwa molingana ndi kupezeka ndi galimoto ya mtengo wapataliyi yomwe ili yobedwa.

Advertisement

Leave a Comment

This site uses Akismet to reduce spam. Learn how your comment data is processed.