A Tembo anali munthu wabwino osati zochotsana muchipani akupanga a Mutharika – Dausi

Advertisement
Malawi Politician Nicholas Dausi

Olira samugwira pakamwa ndipo mneneri wakale wa chipani chotsutsa cha DPP, a Nicholas Dausi, walira mokweza pa mwambo wa maliro wa a John Tembo.

Poyankhula pa bwalo la za masewero la Dedza pamene amaimilira anzawo a Kondwani Nankhumwa amene ndi mtosgoleri otsutsa mu nyumba ya malamulo, A Dausi anati a Tembo anali katakwe pa ndale.

Malinga ndi a Dausi, ukadaulo wa bamboo Tembo pa ndale unaonetsedwa pamene anagwira chipani cha Kongeresi.

“A Tembo anali dolo pa ndale,” anatero a Dausi. “Ndipo iwo samangochotsa anthu mu chipani iyayi.”

A Dausi anayankhula izi pamene iwo ali mu mkokekoke ndi chipani chawo cha DPP chimene chinawathothola. Ambiri amayesa izi zinachitika chifukwa a Dausi anapezeka akukondwa, mpaka kuvina, pa msonkhano wa Kongeresi kumene anakhalitsako ngati membala mpaka anakhalapo wachiwiri kwa a Tembo.

“Ine ndinagwira ntchito ndi a Tembo komanso a Kamuzu Banda. Olo ukayenda nawo ulendo wa kunja, zimaonetsa kuti Tembo ndi katswiri. Wekha umadziwa kuti apa pali munthu apa,” anaonjezerapo chotero a Dausi.

Thupi la a Tembo layikidwa mmanda lero kwawo ku Dedza. Iwo adamwalira ku Lilongwe atadwala kwa nthawi matenda a shuga. Pa ena omwe anali pa mwambo wa maliro ndi mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera komanso mtsogoleri wakale a Bakili Muluzi.

Advertisement