Fizi ku KuHeS yafika pa K1 miliyoni

Advertisement
Kamuzu University of Health Sciences

Sukulu ya ukachenjede ya Kamuzu University of Health Sciences yalengeza kukwera kwa sukulu fizi kuchoka pa K400,000 komanso K550,000 kufika pa K1 million pa chaka.

Malingana ndi chikalata chomwe asayinira ndi a Chikondano Mussa yemwe ndi mlembi wamkulu ku unduna wazamaphunziro, kukweraku ndi kwa ophunzira omwe anayamba Maphunziro awo kuyambira chaka choyamba.

Miyezi yapitayo masukulu ena monga Mzuzu University, University of Malawi adalengezanso kukwera kwa sukulu fizi.

Wolemba: Ben Bongololo

Advertisement