Bambo wazaka 44 ali mchitokosi chifukwa chogwirilira anyamata

Advertisement
A man in Mchinji arrested for raping boys

Bambo wa zaka 44 amumanga ku Mchinji chifukwa chogwirilira anyamata awiri a zaka zosaposera 12.

Wofalitsa nkhani za apolisi ku Mchinji a Limbani Mpinganjira wati bamboyu dzina lake ndi James Makunganya.

Malingana ndi a Mpinganjira, bamboyu aampereka K500 kwa anyamatawa komanso amawaopseza kuti awapha akakawulula kwa makolo awo.

Koma anawa tsiku lina analimba mtima ndikuwawuza makolo awo za chipongwe chomwe a Makunganya amawachitira.

A Makunganya omwe amachokera m’mudzi wa Masautso mdera la mfumu yayikulu Zulu m’boma la Mchinji akuyembekezeka kukaonekela ku khoti kukayankha mlandu wogwirilira ana.

Advertisement