JB atha kufikila m’manja mwa a Polisi


Joyce Banda

Nkhani ija ya ndege ija, zija anamutchula a Lutepo zija, mwinanso zija adanena a Kasambara zija.

Mneneri wa a Polisi mu dziko muno a James Kadadzera ati chilolezo chomwe a Polisi adatenga chowapatsa mphamvu yonjata Mayi Joyce Banda chidakalipo.

Joyce Banda
Mayi Joyce Banda atha kumangidwa ndi apolisi akafika mdziko muno.

A Kadadzera auza olemba nkhani kuti lingaliro lonjata a Banda silidathe chifukwa iwo anakhalitsa kunja.

“Chilolezo chija chilipo ndithu ndipo ndi champhamvu ngati kale,” anatelo a Kadadzera.

Mayi Banda alengeza kuti akubwera kumapeto a sabata ino.

Chaka chatha a Polisi adalengeza kuti atenga chilolezo chowapatsa mphamvu yonjata Mayi Banda kamba koganizidwa pa milandu ingapo.

Discover more from Malawi24

Subscribe now to keep reading and get access to the full archive.

Continue reading