Amangidwa pofuna kuzembetsa anthu

Advertisement
Malawi24

Apolisi kwa Bvumbwe m’boma la Thyolo amanga abambo anayi powaganizira kuti amafuna kuzembetsa anthu okwana 65.

Malingana ndi ofalitsa nkhani pa polisi ya Limbe, Aubrey Singanyama, m’modzi mwa anayi oganizilidwawa ndi a Maxwell Banda a zaka 32 omwe amangidwa pamodzi ndi anzawo ena atatu Lolemba sabata ino.

Singanyama wati anayiwa anapita m’midzi ina m’bomali ndi kuyamba kusonkhitsa anthu, ndikuwakweza bus ya City Tours yomwe nambala yake ndi BU 7217 pomwe akuti amafuna kupita nawo m’boma la Rumphi.

Apolisi ya Bvumbwe atatsinidwa khutu za nkhaniyi, adayiyimitsa itafika pa malo ochitira chipikisheni a Bvumbwe ndipo anayiwa anamangidwa atalephera kufotokoza bwino bwino za komwe akulowera ndi anthuwo.

Malingana ndi a Singanyama, pakadali pano zolinga zomwe anthuwa omwe ndi ana aakazi 12, amuna 14, amai 17 komanso abambo 22, amatengeledwera ku Rumphi sizinadziwike.

Pomwe oganiziridwawa akuyembekezeka kuyankha mulandu ofuna kuzembetsa anthu, apolisi abwezera m’makwawo anthuwa.

Advertisement

Leave a Comment

This site uses Akismet to reduce spam. Learn how your comment data is processed.