Kaya wina afune, kaya asafune, 2025 ndikubweleranso m’boma – APM

Advertisement
Peter Mutharika is politician in Malawi who who was president of Malawi from 2014 to 2020

Inu nonse amene a Peter Mutharika simukuwafuna, yang’anani kumbali. Nonse aja olemba kuti “APM my vote”, senderani chifupi. A Mutharika lero abwerezanso kuti chaka cha mawa akubwelera ku Sanjika.

Mtsogoleri wa chipani chotsutsa cha DPP amene mmbuyomu amaoneka ngati wasiya za ndale asanalengezenso kuti basi akubwelera wauza anthu ku Mangochi kuti 2025 iye akuima ndipo awina. A Mutharika analankhula izi pamene anapereka katundu kwa asilamu ena amene akusala kudya m’bomalo.

Peter Mutharika speaking in Mangochi in March 2024
Mutharika: Ndiyimanso

Malinga ndi a Mutharika, iwo ati pa chisankho cha chaka chamawa, ayima ndipo apambana. Ati akapambana boma la Mangochi azalisintha, mpaka kumamgako bwalo la ndege.

A Mutharika amene anatuluka ndi Mayi a kunyumba kwawo anauza anthu amene anakumana nawo kuti boma la Tonse liribe utsogoleri. Ati a Chakwera sakudziwa chomwe akuchita. Ndipo dziko lino ngati lingayambe kuona njira ya chitukuko ndiye ndi pamene iwo abwelere m’boma basi.

Mawu a Mutharika adza pamene yabukanso nkhani yokhazikitsa lamulo lofuna kuletsa anthu okalamba kuyimira ma udindo a ndale, monga mtsogoleri ndi phungu.

Mu nyumba ya malamulo munayamba mpungwepungwe pomwe zinadziwika kuti a Welani Chilenga akufuna kubweletsa lamulo lokhudza zaka poimira udindo. Anthu ambiri anena kuti lamuloli likufuna kukhaulitsa a Mutharika omwe akuyembekezereka kukhala ndi zaka 85 chaka chamawa.

Advertisement

Leave a Comment

This site uses Akismet to reduce spam. Learn how your comment data is processed.