Tisaleme kuthandiza anthu omwe akhudzidwa ndi njala – atero mai Joyce Banda

Advertisement
Former President Joyce Banda in Zomba

Mtsogoleri wakale wa dziko lino, a Joyce Banda, apempha boma ndi mabungwe omwe akugawa chimanga kwa anthu omwe akhudzidwa ndi njala m’dziko muno kuti achite machawi kufikira madera ambiri anthu ambiri akhudzidwa ndi mavuto osowa chakudya.

A Banda anayankhula izi ku Domasi boma la Zomba kumene anali nawo pa mwambo omwe bungwe la Shepperd Bushiri la Goshen Farms limagawa chimanga cholemera 50 kgs  kwa anthu amene akhudzidwa ndi njala.

Iwo anati: “Cholinga cha ntchitoyi ndi kupulumutsa anthu omwe ali pa Mavuto osiyanasiyana kuphatikizapo chakudya”

Irene Sawanga and Godwin Chimbewa ndi ena mwa anthu omwe alandira chimangachi ndipo anati izi zapatsa mphamvu zokagwira tchito za kumunda.

Sawanga anapereka chitsanzo kuti ku munda wake wazula chimanga chonse chomwe chinauma ndi dzuwa ndikubzalamo mbatata.

“Ndikupanga izi kuti munda wanga ndipindule nawo ngakhale chimanga chakanika” antero

Wolemba: Peter Mavuto

Advertisement