Malipoti akuti Nankhumwa akubwela ndi chake chipani: PDP

Advertisement
Kondwani Nankhumwa Malawi

Nonse othodwa ndi zipani zonse zilipo pano, ena chabe ongokhala okondwa ndi bambo Kondwani Nankhumwa ndipo mumafunitsitsa atalamula dziko lino, musataye mtima kwenikweni. Chipani chatsopano chikubwela. Okamba akuti ndi cha a Kondwani Nankhumwa. Dzina lake ndi PDP, People’s Development Party.

Malinga ndi Malipoti amene Malawi24 yamvetsedwa, ma mulumuzana ena amene anali a chipani cha DPP ati akhala akuchita mikumano kukonzekera kulembetsa chipani chawo chatsopano.

“Kwambiri akungodikira kuti mkumano wa aphungu uthe, akatero basi ndi watsala watsala, ma kampeni akuyambika,” anatero mkulu wina amene ali nawo pa kalikiliki opanga za chipani chatsopanochi.

Zikalata zina zimene taona zikusonyeza kuti akuluakulu a chipanichi akutenga maina a mmaboma onse a dziko lino kuti akwanitse zofunika polembetsa chipani.

Mu chikalata chimene taona, a Nanariwa Nanguwo amene mmbuyomu amadziwika ngati mmodzi okonda chipani chotsutsa cha DPP ndiwo asayinila ngati mlembi wamkulu wa chipanichi. A Nanguwo akhalanso akukhala patsogolo pa nkhani za Mulhakho wa Alhomwe.

Munthu amene watitsina khutu ku zochitika za mu chipani chatsopanochi wati mtsogoleri wake ndi a Kondwani Nankhumwa amene anadomoledwa ku DPP. Cholinga chawo ati ndi choti azakwaniritse masomphenya awo a dziko lino akalowa m’boma.

Mmbuyomu a Nankhumwa adalengeza kuti adziwitsa mtundu wa a Malawi za zomwe achite atachotsedwa mu chipani. Atatero a mzawo amene anachotsedwa nawo a Msonda analengeza kuti iwo tsopano akumanga maziko a chipani chatsopano. Koma a Nankhumwa anatsutsa za nkhaniyi.

Padakali pano, a Nankhumwa adakamang’ala ku bwalo lamilandu za kuchotsedwa kwawo mu chipani.

Advertisement