Chakwera aboola mtambo lero wa ku DRC

Advertisement
Malawi President Lazarus Chakwera

Mtsogoleri wadziko lino a Lazarus Chakwera akuyembekezeka kuboola mtambo lero pa ulendo opita mdziko la Democratic Republic of Congo (DRC).

A Chakwera akukawonelera mwambo olumbilitsa mtsogoleri wadzikolo a Felix Tshisekedi Tshilombo yemwe wangosankhidwanso  kumene komanso akukakambilana ndi a Tshisekedi zokhudzana ndi asilikali a Malawi omwe akugwira ntchito yosungitsa bata ku DRC.

Malingana ndi kalata yomwe yatulutsa ndi unduna woona za ubale pakati padziko lino ndi mayiko akunja, a Chakwera analibe malingaliro opita ku DRC koma ayenda chifukwa chakuti ayitanidwa ndi a Tshisekedi.

Mtsogoleri wa dziko linoyu anyamuka 11 koloko m’mawa uno kudzera pa bwalo la ndege la Chileka munzinda wa Blantyre ndipo akuyembeka kudzabwelera kuno ku Malawi lamulungu.

Aka nkoyamba a Lazarus Chakwera kuboola mtambo kutuluka mdziko lino chilengezeleni kuti wayimitsa maulendo ake mu November chaka chatha. A Chakwera adanena  kuti adzayambilanso kuyenda mu April  chaka chino ndicholinga chakuti chuma cha boma chisaonengeke.

Wolemba: Ben Bongololo

Advertisement

One Comment

Comments are closed.