
Anthu a mipingo ndi ena onse amene akudana ndi lamulo loti amayi aziloledwa kuchotsa pakati asayese Mafumu ali mbali yawo.
Malingana ndi Mfumu Yaikulu Lukwa ya a Chewa, Mafumu akugwilizana ndi lamulo loti amayi aziloledwa kuchotsa pakati.
A Lukwa amene ndi mlembi wamkulu wa bungwe la Mafumu ati iwo monga Mafumu ali okonzeka kuchita zionetselo ngati aphungu akane kukambilana za lamulo limeneli.
“Takonzeka kuvala mikanjo yathu ya ulemelero ndi kupita ku nyumba ya malamulo komweko kukawauza a phungu kuti nkhani imeneyi tikufuna ikambidwe,” anatelo a Lukwa.
Iwo anaonjezelapo kunena kuti Anthu amene akudana ndi lamulo lochotsa pakati sanakhale ndi nthawi yowelenga zimene lamulo limeneli likukamba.
“Nkhaniyi ena angoyankhula mwaphuma, sanawelenge za lamulo limeneli ndi komwe. Anthu otelewa asatisokoneze,” anaonjezelapo.
Lamulo lovomela amayi kuchotsa pakati linakolela moto pakatipa a mipingo atachita chionetselo chokana kuti pakhazikitsidwe lamuloli.
312 thoughts on “Mafumu akufuna amayi aziloledwa kuchotsa mimba – atelo a Lukwa”
Comments are closed.










Mfumu yopusa ingathe kutero koma yozindikira singalole zopusazo ndipomwe tidziwe mafumu opusa ndi ochenjera
Ayambe achotsa yakeyo kenako azimayiwo
Mafumu otumidwa Ndi satana kuti athandize nawo pa nkhani yosocheretsa anthu.
Mbuzi za anthu zimenezi, chifukwa chani koma
Musatiwawitse mutu ndi nkhani za nkutu ngati imeneyi mamfumu sakudziwa kuti kodi kuseli kwa mchitidwe umenewu kuli chani akapatsidwa timalawasi basi asintha zolankhula.stupid