Awalamula kuti apereke K2.7 miliyoni kamba kopezeka ndi chamba

Advertisement
Malawi Chamba suspects

Anthu atatu m’boma la Dowa alamulidwa kuti apereke ndalama zokwana K2.7 million aliyense kapena kukaseweza ndende kwa miyezi yokwana makumi atatu (30) atapezeka olakwa pa mlandu opezeka ndi chamba.

Anthu atatuwa omwe ndi a Charles Kanyenga a zaka, 36, a Precious Elisa a zaka 29 komanso a Foster Wilimoti azaka 24 zakubadwa.

Majisitileti Talakwanji M ‘dala yemwe ndi wa bwalo la milandu la Mponela m’bomali ndi yemwe wapereka chigamulochi.

Makosanawa anagwidwa ndi apolisi pa trading center yotchedwa Mlengwe m’bomali sabata latha.

Wolemba: Ben Bongololo

Advertisement