Akaidi ku Kasungu lero akumbukila maufulu achibadwidwe

Advertisement
Malawi Human Rights

Akaidi pa ndende ya Kasungu lero pa 5 December anali pa mwambo okumbukira ufulu wa chibadwidwe pa mutu woti “Ulemu, Ufulu ndi Chilungamo kwa Onse.”

Ndipo ngati njira imodzi yofalitsira uthengawu, iwo anagwiritsa ntchito maluso osiyanasiyana pa mwambowu.

Kudzera musewero lomwe  iwo anachita, iwo ati anthu ochuluka amamangidwa ndikugamulidwa kukaseweza ndende ngakhale kuti anali ndi osalakwa kamba kakuti sadziwa maufulu awo.

Seweroli linapitilizanso kufotokoza ndikupempha kuti mabungwe osiyanasiyana komanso boma likuyenera kutengapo mbali powonetsetsa uthenga wa maufuluwa ukufalitsidwa mokwanira.

Chikondwererochi akuchititsa ndi a bungwe la Paralegal Advisory Service Institute (PASI) ndi thandizo lochokera ku Irish Rule of Law.

Ndende ya Kasungu ndi imodzi mwa ndende zomwe zili ndi chiwerengero cha akayidi ochuluka. Ndenndeyi imasunga akayidi 548.

Wolemba: Ben Bongololo

Advertisement