Bushiri wapempha mgwirizano pa ntchito yothandiza ovutika

Advertisement
Bushiri wapempha mgwirizano pa ntchito yothandiza ovutika

Mneneri Shepherd Bushiri yemwe ndi tsogoleri wa mpingo wa ECG-The Jesus Nation, wati pomwe lafika vuto la njala mdziko muno, ndipofunika kuti azipembedzo komaso anthu andale ayiwale kaye zakusiyana kwawo pa zikhulupiliro komanso pandale ndikuyamba kuthandiza a Malawi omwe akugona kumimba kukulira malikhweru.

Mneneri Bushiri walankhula izi Lamulungu kwa Mkando m’boma la Mulanje komwe anapita kukapitiliza ntchito yomwe wakhazikitsa posachedwapa yogawa chimanga kwa anthu omwe akhudzidwa ndi njala ya dzaoneni yomwe yakhudza madera ambiri mdziko muno.

Poyankhula pa chikhwimbi cha anthu omwe anakhamukira pa bwalo la masewero la Nkando, mneneriyu wati wayenda m’madera ochuluka m’dziko muno ndipo wati zinthu sizili bwino kotelo ndikofunika kuti pakhale kugwirana manja pa ntchito yothandiza anthu omwe akhudzidwa ndi njalayi.

Bushiri wati ino sinthawi yolimbana ndi ndale kapena zikhulupiliro koma kugwirana manja populumutsa miyoyo ya a Malawi omwe ena akumagona atangodya zikhawo, njele za tchire komaso zinthu zina zomwe zikumapeleka chiopsezo ku miyoyo yawo.

“Ndipemphe anthu tonse kuti chonde, ino sinthawi yoti tizilimbanaso ndi ndale kapena kusiyana kwathu pa zikhulupiliro. Anthu akuvutika m’midzimu nde tikungoyenera kuyiwala kaye za kusiyana kwathu ndicholinga choti ntchito yothandiza anthu omwe akhudzidwa ndi njalayi igwiridwe mosavuta. Chonde tiyeni tigwirane manja,” watelo Bushiri.

Loweluka, Bushiri anali m’boma la Thyolo komwe anagawa chimanga kwa anthu opitilira 1200 ndipo pano chiwerengero cha anthu omwe wawapatsa chimangachi mdziko muno chapitilira anthu  50,000.

M’neneri Bushiri wanenetsa kuti iye sakufuna kuti ndondomeko yake yogawa chimanga ilowe ndale ndipo wati madera omwe akugawa chimanga sakumatengera kuti kuli anthu otsatira chipani chanji.

Posachedwapa Bushiri anakhazikitsa ntchito yogawa chimanga chochuluka matani 17,000 chomwe ndi cha ndalama zosachepera 14 biliyoni kwacha ndipo chomwe akuti achigawa kwa anthu opitilira 1,000,000.

Advertisement