Mayi wamangidwa kamba kogwilirira mwana wazaka 16

Advertisement

Mayi wazaka 38 yemwe dzina lake ndi Takondwa Banda ali m’manja mwa a polisi ku Kasungu kogwirira mwana wammuna wazaka 16 ndi kumupatsila matenda opatsilana pogonana.

Mneneri wa polisi ya Kasungu Joseph Kachikho wati izi zinachitika mu mwezi wa Okotabala chaka chino.

A Kachikho ati mnyamatayu analembedwa ntchito yogwira kumunda kwa a Banda ndipo amagona ku khitchini.

Kenaka tsiku lina, Banda anauza mnyamatayu kuti akagone m’nyumba mwake. Apa Banda anayamba kumuonetsa mwana uja makanema olaula kenaka anamukakamiza kugona naye.

A Banda anapanganso zomwezi tsiku lina ku tchire ndipo mwana uja anakatula nkhaniyi ku polisi.

Malingana ndi a Kachikho, mwanayu atamutengera ku chipatala cha Kasungu anamupeza ndi nthenda ya chindoko yomwenso mayi Banda anawapeza nayo.

Mayi Banda akuyembekezeka kuonekera ku bwalo la milandu pa mulandu wogonanana ndi mwana.

Advertisement