Anabwela atayaka kapena? A Kongeresi ati za mgwilizano amayankhula Chilima ndi zamkutu


Zija amayankhula wachiwili kwa mtsogoleri wa dziko lino a Saulos Chilima zoti anagwilizana ndi a Lazarus Chakwera kulandilana mu 2025 ati ndi zamkutu komanso zongopeka. A Kongeresi alibe mgwilizano umenewo.

Malingana ndi mlembi wamkulu wa chipani cha Kongeresi, a Eisenhower Mkaka, chipani cha MCP chilibe ma pepala a mgwilizano amene akukamba a Chilima.

Iwo anena izi pa msonkhano wa atolankhani omwe anachititsa ku likulu la chipanichi ku Lilongwe pofuna kuthililapo ndemanga pa zimene a Chilima anaudza dziko la chisanu madzulo.

Malingana ndi a Mkaka, chipani cha MCP chilibe buku la mgwilizano limene a Chilima amawelenga.

A Chilima pachisanu anadzudzula mkhalakale za MCP ati kamba kodzetsa mpungwepungwe mu mgwilizano wawo pomati a Chakwera ayimanso 2025.

Follow us on Twitter:

Discover more from Malawi 24

Subscribe now to keep reading and get access to the full archive.

Continue reading