Flames yafika ku Tunisia

Advertisement
Flames

Anyamata anu mwawatuma ku Tunisia aja afikako koma kwatsala ndikubweletsa zotsatira tsopano.

Timu ya dziko lino yampira wamiyendo yatera mdziko la Tunisia lero kudzera pa bwalo la Ndege la Tunis-Carthage International, pomwe ikuchalira kuvungumulana ndi timu ya dzikolo Lolemba lino.

Timu ya dziko lino yomwe yanyamuka dzulo, idzikapita pa bwalo la Hammadi Agrebi ikuchokera kosakazidwa ndi Namibia 1-0, ndipo idzikakumana ndi Tunisia yomwe ili pa nambala 1, pomwe Malawi ili pa nambala 4 onse mu guru H.

Kuyambira pa mndandanda momwe akuchitira bwino, mu guru H muli ma timu a Tunisia, Namibia, Liberia, Malawi, Equatorial Guinea ndi Sao Tome and Principe.