![Patricia Kaliati - UTM](https://malawi24.com/wp-content/uploads/2024/05/United-Transformation-Movement-UTM-750x400.jpg)
Yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha United Democratic Front (UDF) ku chigawo cha ku m’mawa a Hashim Banda ati masomphenya a chipani cha United Transformation Movement (UTM) anawakopa ndi chifukwa alowa chipanichi.
Poyankhula pa msonkhano wa ndale omwe chipanichi chinapangitsa pa bwalo la Chinamwali ku Zomba a Banda ati nzosabisa kuti dziko likuyenera kudziwa kuti mfundo ndi masomphenya a chipani cha UTM ndi a mphamvu komanso ali ndi kuthekera kosintha zinthu, iwo ati zipani mdziko muno zimawafikira kuti azitumikire pamene anangotula pansi udindo ku UDF koma anasankha masomphenya a tsogolo ndi chifukwa alowa UTM.
A Banda omwe mu masankho a 2019 anapikisana nawo pa mpando wa phungu wa dela la pakati m’boma la Zomba ati akapikisana nawonso pa mpandowu pa masankho amene akubwera chaka cha mawa ndipo atsimikiza kuti akapambana.
![Patricia Kaliyati](https://malawi24.com/wp-content/uploads/2024/05/Patricia-Kaliyati-UTM.jpg)
Mlembi wamkulu wa chipani cha UTM a Patricia Kaliati ati manifesito a chipanichi ndi kudzakwanilitsa zomwe analonjeza kale mu manifesto yawo, ndipo kubwera kwa adindo akulu-akulu ena ku chipanichi ndi umboni wa kuthekera ndi tsogolo lomwe chipanichi chili nako.
A Kaliati ati mavuto amene dziko lino likukumana nawo akuyenera kutha chipanichi motsogozedwa ndi mtsogoleri wawo a Saulos Chilima akadzalowa m’boma chaka cha mawa ndipo ati manifesito yomwe ikugwiritsidwa ntchito pakadali pano si a UTM.
Pa msonkhanowu anthu ena oposa makumi asanu alowa chipanichi kuchoka ku zipani za DPP ndi UDF.