Khwimbi latayira kamtengo Yobu Kachiwanda ndi DCCMS ulosi wamvula utapherezera

Advertisement
Khwimbi latayira kamtengo Yobu Kachiwanda ndi DCCMS ulosi wamvula utapherezera

Kutsatira ulosi omwe nthambi yoona za nyengo mdziko muno inachita ponena kuti mvula iyamba kugwa pa 1 February mwezi uno, tsopano a Malawi ambili ayamikila ulosi wanthambiyi pamene mvula yagwadi m’madera ochuluka ngati momwe nthambiyi inaloselela.

Dzana mneneri wa ku nthambi yoona za nyengo a Yobu Kachiwanda anatsimikizira mtundu wa a Malawi ponena kuti mvula iyamba kugwa mwezi uno pa 1 February pamene pachigawo cha pakati komanso kumwera kwa dziko lino kwakhala kopanda mvula pafupifupi masabata awili.

Kugwa kwa mvula pa 1 February a Salima ndi Kasungu kunafanana ndi zomwe nthambiyi inalosera zomwe zapangitsa a Malawi ambili kutayira ka mtengo nthambiyi.

Pakadali pano alimi okhala mboma la Salima ati ndiwosangalala kamba kamvulayi popeza ng’ambayo ikadatha kuwononga mbewu zawo m’minda pamene zinayamba kuwuma.

Wolemba: Ben Bongololo

Advertisement