![Sangwani Phiri](https://malawi24.com/wp-content/uploads/2016/12/Sangwani-Phiri-750x400.jpg)
A ku unduna woona za chilengedwe, mphamvu ndi migodi ati iwo satopa kulimbana ndi anthu onse amene ali pa kalikiliki kufukula mchenga.
Malinga ndi a Sangwani Phiri amene amayankhulila undunawu, iwo ati undunawu ndi okhumudwa ndi khalidwe lovuula mchenga maka m’mbali mwa mtsinje.
![Sangwani Phiri](https://malawi24.com/wp-content/uploads/2016/12/Sangwani-Phiri.jpg)
Iwo ati boma ndi lokhudzika ndi mchitidwe umenewu kamba koti umaononga chilengedwe.
A Phiri ati ngati boma, sanyengelela anthu onse opezeka akuchita makhalidwe amenewa.
Iwo apemphanso mafumu ndi a Malawi onse kuti akhale okonda dziko lawo ndipo agwilizane ndi boma pothetsa mchitidwewu.