Kodi munthu akamayendera galimoto yabwino ndekuti ndi wa Satanic? – Gwamba

Advertisement
Gwamba

Oyimba chamba cha Hip-Hop koma mwauzimu, Gwamba atafunsidwa funso lokuti “Kodi mumakwanitsa bwanji kukhala wa Satanic” nayenso anayankha ndi funso “Kodi munthu akamayendera galimoto yabwino nde kuti ndi wa Satanic?

Anayankhula izi mukucheza kwawo ndi Blesikwa pa kanema yotchewa Pakaya yomwe imawulutsidwa pa tsamba la pa utatavo la Youtube.

Blesikwa anamukanira Gwamba kuti iyeyo sioyankha mafunso koma ofunsa koma sizinaphule kanthu chifukwa oyimba wa Lilongwe-yu adapitiliza kufunsa “iyayi ndifuna ndidziwe mukamati Satanic mumatanthauza chani?

Ngakhale kuti nkhaniyi sinapitilire koma anthu ambiri pa masamba a mchezo maka pa Facebook akhala akumunena Gwamba kuti ndi wa Satanic pa zifukwa zomwe akuzidziwa okha zomwe zinapangitsa Besikwa kuti afunse fusoli.

Ngakhale izi zili chomwecho, anthuwa anakambirana zambiri pakucheza kwawo kuphatikizira mphekesera zomwe zakhala zikumveka kuti Gwamba ndiosamphunzira kamba koti nyimbo zake sagwiritsa ntchito chingerezi ngati oyimba ena a Hip-hop achitira.

“Ndili ndi tsamba la sukulu ya ukachenjede ‘Degree’ ya credit koma sindinagwiritsepo ntchito ndipo sindikudziwa kuti ndinalisiya kuti,” anatero Gwamba mwathamo.

Komatu anatsindika kuti Degree yomwe anapanga ya za malonda imamuthandizira kuyendetsa bwino mbali yayikulu yamayimbidwe ake.

Gwamba anadziwika pafupifupi zaka zoposera khumi zambitazo ndi nyimbo monga ” Ndidikira” “Tikakumane Kumadzi” kungotchula zochepa chabe.

Loweruka likudzali, Gwamba wakhonzanso phwando lamayimbidwe lomwe likutchedwa “The Best of Gwamba Concert” ku bwalo lazamasewero la Civo ku Lilongwe kukondwelera zaka khumi ndi zisanu zamayimbidwe.

Advertisement

Leave a Comment

This site uses Akismet to reduce spam. Learn how your comment data is processed.