![Edgar Lungu](https://malawi24.com/wp-content/uploads/2016/05/Edgar-Lungu-624x400.jpg)
M’tsogoleri wakale wa dziko la Zambia, a Edgar Chagwa Lungu, wati zitengera a Malawi kukavotera m’tsogoleri amene ndi wongoyeselera zinthu kapena wodziwa zinthu, maka pachisankho chomwe chichitike chaka chamawa m’dziko muno.
A Lungu ayankhula izi pa tsamba lawo la m’chezo la Fesibuku dzulo pa 16 May 2024.
M’mawu ake lungu anati akumva kuti a Malawi adzavota chaka chamawa ndipo anthu ambiri adzasankha pakati pa paukadaulo pochita zinthu kapena kungochita zinthu moyeselera.
Pomaliza a Lungu anati akufunira zabwino abale ndi alongo kuno ku Malawi ndipo iye analangiza anthu m’dziko muno kuti akhale amtendere komanso otetezeka.