Mlandu wa Lester Maganga ulowanso mu bwalo mwezi wamawa


Mlandu wa Lester Maganga ulowanso mu bwalo mwezi wamawa- Malawi24

Oweluza Milandu ku bwalo lalikulu a Mzondi Mvula apeleka chitsogozo chakuti mulandu wa a Lester Maganga ukhala ndi masiku khumi ndi anayi (14) kuti umvedwe ndipo kuti oganizilidwawa akakhalebe akusungidwa m’manja mwa a chitetezo kufikila mtsogolo..

Mu kumvedwa kwa mulanduwu lero ku bwalo lalikulu mu mzinda Lilongwe a Lester Maganga akana kuti iwo si olakwa pa milandu yonse iwiri yomwe akuwaganizira.

Oweluza Mvula wati tsopano mulanduwu udzayamba kumvedwa kuyambila pa 13 February mpaka pa 7 March chaka chomwechino zonse zikakhala mchimake.

Oyimilira mbali ya boma pa Mlanduwu awuza bwaloli kuti potsatila kukana kwa a Maganga milanduyi iwo abweletsa mboni zokwana khumi ndi zisanu (15) ndipo iwo anawonjezera kuti mboni zonse zilipo.

A bwalo alamulanso kuti aboma atengele oganizilidwawa ku chipatala kuti akawayeze ku kalikonse kokhudza ubongo m’masiku asanu ndi awiri akudzawa kuti mulanduwu ukayamba usakhale ndi zosokoneza.

A Lester Maganga akuwaganizila kuti adapha a Allan Wittika chaka chatha, Ndipo a bwalo akhala akuwayimba mulandu wakupha komanso opezeka ndi futi komanso zopolopolo popanda chilolezo.

Discover more from Malawi24

Subscribe now to keep reading and get access to the full archive.

Continue reading