A Kongeresi ati akola chambo, a DPP ati ndi chule ameneyo

Advertisement

Eni ake akolawo ali ndi chimwemwe kuti akhwasula, kuti mavoti onse a Kum’mwera kwa mzinda wa Blantyre tsopano akhala awo. Koma kwa aneba awo ndiye kuli phwete.

Pamene ndale zafika pa chi inde inde, chipani cha Kongeresi chalengeza kuti chalandila mu chipanichi Anong’a Fischer Kondowe.

a Mia kulandila Fischer Kondowe mu MCP.

Kondowe amene ndi katswiri wa mpira wakhala akulengeza kuti iye wapanga chisankho choyamba ndale. Iye wati 2019 akhala akupikisana nawo pa mpando wa uphungu ku dera la Kum’mwera mu Blantyre kumene phungu wake pakali pano ndi a Allan Ngumuya.

Pamene Kondowe amalengeza za maloto ake, iye sanatchule chipani chomwe ayimile koma tsopano zadziwika.

Kondowe walandilidwa ku chipani cha Kongeresi ndi Bambo Sidik Mia amene akuoneka kuti atha kuzakhala wachiwili wa Bambo Chakwera mu 2019.

Anthu a Kongeresi akuoneka osangalala pa Facebook ndi kubwela kwa Anong’a. Zikuoneka ngati kwa iwo Anong’a ndi Khang’a amene awabweletsele mavoti.

Pamene a Malawi24 tinalemba nkhaniyi mu chizungu, anthu angapo okonda Kongeresi ananyadila.

“Mwachita bwino Jah man, mwasankha chipani chowina,” analemba choncho a Steve Nzati.

A Fred Matabwa nawo anamuyamikila kuti Kondowe ndi olimba mtima ndipo wapanga chisankho cha nzeru.

Koma anthu ambiri a DPP aseka ndi ganizo la Kondowe.

Advertisement

67 Comments

  1. zomwe boma lakonza ndi zakuti anthu okwana 300,000 achigawo chapakati salandila ma I.D. kotelo sazaloledwa kuvota ,kima a mcp palibe chomwe akuziwa ,nthawi yachisankho ndi pomwe wina azalile chokweza kuti mayo!!!!! andibela mavoti ine . pomwe chigawo chakumwela aliyense alandila ma I.D. ndicholinga chozavota mwaunyinji.

  2. MCP siingawine,magazi akadalibe mmanja.Ng’ona ndi mboni.Dpp isatinyase ma blackouts awonjeza.Aise Kamlepo,taimila ndi Chilima tizakuvotela.

  3. Alibe certificate ya 4 komaso munthu wosakwatila does not know the responsibility fist he has to marry and have children then practice to be responsible.

  4. Bola Osandibela Vote Dpp Sindinapindule Nayo Mtukula Pankhomn A D R Kundimana Ngati Siine Malawi Nthawi Yanga Yakwana Nane Ciziwe Mchipande

  5. kkkkk koma2019 mukuchimilabwanjiandalenu musatayemtima zotikuli chule kapena chambo ziwanikutimwapangachisakhononkha chobetsandalamazanuzo ulendowokabam.bomasiwaufupi mukuyenelakutidishapopangakapeni kutitikupatseni mpandowokabelaboma ndikukumbutsekuti cash gent meizegent heth gent zotsezotilinazo kale musakabe ndalamachimangamakwala enawaanatibela kale?

  6. AKAFUKUFUKU ANAPANGA KALEKAFUKU FUKU KUTI MCP IZAWINA 2019 MOTELO UMBONI WOTI IWOWANDIAKASWILIDI UNAWONEKA PA MABAELECTION PAMENE MCP INATENGA MIPANDO 2 KUMWELA 3 PAKATI .A DPP ANANGOTENGA UMOZIBASI WAKHAMSALA

    1. U clever wa dpp uli pati, rigging will be thwarted, ma alliancy akukanika, dividing mcp zikukanika. Komanso osaiwala mcp ya Tembo ndi chakwera ziwiri zosiyana team ya chakwera ndiyochangamuka kwambiri tembo was dull nchifukwa ankangomubera.

    2. What clever are u trying to say? If so all these past 13yrs why didn’t they plan for electrical power shortage that have affected our poor nation this time?

    3. MCP singawine.Mukuyesatu inu.Dpp has a winning DNA in their blood.Ur Malawi Clockdiles Party has their favourite song titled “atibela”.Get ready kuliranso ulendo uno.Tiziuzana zoona.zoti MCP ingachotse Dpp ndi maloto chabe.Mulira

  7. Ukunama aisee ulendo siuno mcp ilulowa paliponse adawina bwanji wa mcp ku nsanje nanga kundilande,madela amenewa ndi chigawo cha pakati? Samala ndizolankhula zako udzalira nao limodzi anzako ADPPwo.

    1. DPP ? Tamavomerezani kulephera inu, kakaka mukufuna muchoke mutamubera ndani ku DPP? Ndale zakumalawi dyera too much aMalawi.

  8. Ozalila 2019 achulukatu mpaka Jah Man akufuna kuzathandizila kulila ndi a MCP,,, Kugwesa DPP nkulinga utakhala wakumwela

  9. Msanje lalanje kuti boooooooooom chule anangodumphila chakonko chambo balala mpaka 5 kwa 0 ndiye poti simutha kulankhula mumalankhula chizungu zikuvutani ife tili Nyodooooooooo!!!! Tukutibula Chambo hahahaha

  10. Jahman Wambwita Akanaima Ngati Independent Zikanayenda!Koma Mcp Yamagaziyi?Komanso Mp Amayenera Kukhala Odzisamala Osamba Awa Umawakhala Ndimpira Omwewo!Peter Mponda Emweyo.

    1. Iremind U Dpp Ilowaso M’boma Abale Akowa Amcp Akungokhalira Kukangana Nde Zitheka? Ku North Mcp Akasiya Msowoya kukhala vc basi support imene ukunena ithera pomwepo.

    2. Watson,Mukuyambitsa ndinu a DPP koma ndi mbwererera mwakhala mukuchitazi,umbava mkati osamva chisoni ndi mtundu wa amalawi,kumanyada chifukwa muli pamwamba mumtengo now nthawi ikukwana mwayamba kudetsa ena?? Nkasa tu anayimba pa dana apo,KULIRA KWA DZIKO,poyambapo anati sindidziwaaa kuti ndichani,koma anaona anthu osauka akulira,ndipo amphawi aliladi ndipo akanalira kamba ka nkhanza zanu inu a DPP,umbava wanu wafika pena,ndipo Nkasa yo sanasiyele pompo anati,Sindidziwaaa kuti ndichiani,koma ndinaona Kuphiri/kubomako akulira,ndipo nthawi yake ndiimeneyi mulira inu aM’boma chifukwa m’malawi wa nzeru sangayelekeze kukuvoterani. Blv me Malawi uyu si wakale and MCP yakale si yalero utati uwone palibe ngakhale m’modzi wakele amene alipo ku MCP ya lero. Mudziona

    1. Ukukhala ngati zoti anabera chisankho sukudziwa bwanji? Ndiwe mlendo kodi? Dilu PhwiPhwi nde Chaninso ???

    1. Pepani bwana ine siwandale koma ndingoyankha pokhapa school ndi utsogoleri zinthu ziwiri zosiyana ndipo mchaka amalawi ambiri akunzuzika chifukwa chowona ngati school ndi yofunikira kwambiri pautsogoleri chitsanzo ndi izi zikutikanikazi ati a professor Zaziiiiii zeni zeni

  11. Koma game ya ndale ndiyovuta kwambiri imafunika kusamalitsa chikufunika apa Dpp ndikuchelenjela basi chifukwa mwamuna nzako mpachulu.

Comments are closed.