![Dausi](https://malawi24.com/wp-content/uploads/2017/04/nicholas-dausi-750x400.jpg)
Ngakhale a bungwe loona za madzi mu Lilongwe la Lilongwe Water Board linanena kuti madzi a ku Area 18 atha kumwedwa tsopano, nduna ya zofalitsa nkhani a Nicolas Dausi ati iwo sangamwe madzi otuluka ku deralo.
![Sidik Mia](https://malawi24.com/wp-content/uploads/2016/02/nicolas-dausi.jpg)
A Dausi ananena izi lamulungu pocheza ndi mtolankhani wina pa wailesi.
Pa nkhani ina imene iwo anafunsidwa monga mneneri wa boma inali yokhudzana ndi madzi a ku Area 18.
Iwo analangiza anthu a ku Area 18 kuti amvele langizo la anthu a ku Water Board amene akunena kuti madzi a kumeneko ndi oyenera kumwedwa tsopano.
Koma atafunsidwa ngati iwo angamwe madziwo, a Dausi anachita njengunje ndi kunena kuti nkhani imeneyo akuyenela kufunsidwa ndi a ku Water Board.
Iwonso anatsindika kuti sangamwe madzi a ku 18.