Tulani pansi – alangizi a Mutharika auzidwa kamba kobisa matenda a Tate wa dziko lino

Advertisement
John Chisi

Alangizi a mtsogoleri wa dziko lino alamulidwa kuti atule pansi udindo wawo ati chifukwa akhala akubisa matenda a mtsogoleri wa dziko linoyu.

Izi zanenedwa ndi mtsogoleri wa chipani cha Umodzi a John Chisi.

A Chisi ati alangizi a mtsogoleriyu akumulangiza kuti azipanga zinthu zolakwika zomwe zina mwa izo ndi kubisa matenda amene akuoneka kuti avuta mtsogoleriyu.

John Chisi
Chisi; Mutharika sakulangizidwa bwino.

“Ngakhale ali mtsogoleri wa DPP, iyeyu ndi mtsogoleri wa dziko linonso,” anatero a Chisi. “A Malawi ayenela kudziwa za umoyo wa mtsogoleri wawo, osati kunamizidwa iyayi.”

A Chisi analankhulaponso pa ndemanga zimene wathila mtsogoleri wa zipani zotsutsa mu nyumba ya malamulo amene alinso mtsogoleri wa Kongelesi a Lazarus Chakwera amene pamodzi ndi a Uladi Mussa, mtsogoleri wa chipani cha Peoples’, amati a Mutharika atule pansi udindo.

“Tiyeni titsogoze mapemphero kwa mtsogoleri wathu, tisakhale ndi dyera pa udindo,” anatero a Chisi.

A Mutharika anafika mu dziko muno lamulungu akuoneka odwala. Iwo amakanika kugwiritsa ntchito dzanja lawo la kumanja zimene zinatsimikizila anthu ambiri kuti mkuluyi ali mdziko la Amereka anadzela kuchipatala.

Advertisement

260 Comments

  1. AChisi sumudachenjerebe mommuja.Paja ndinu okanika.Zomwe mwayankhulazo sizikumveka vomerezani inu siwandale koma wapanado

  2. ZIZAKHALA BETA KAPENA KUTI ZIZAKHALA BWINO POKHA POKHA MWINI DZIKO ATABWERA KUZAWERUZA DZIKO RINO MURIRI WACULUKA M’dziko lamalawi.

  3. Amalawi samalani nawo maactivist amenewa. Akupheran ufulu wano wofuna kuziwa zochitika ndi olamula bomawa. This is like barringvsm1 the right to info.NO TO THAT REGULATION. Atumidwa komanso alandira kenakake

  4. munthu akamdwala salengeza koma akamwalila ndiye ndee tavetse atsogoleli athu zimeneakunena osati m’pakani atulepasi undindo chifukwa cha matenda iyayi.

  5. nonse mwaika ndemmanga apa ndimbuzi zaanthu,ndikalelija timakhala anthu mu nziguduli kuti tisamawonepatali,lelo ndiufulu wamalawi kuziwa chikuchitika mzikolawo,timamva pa radio kuti amugabe akudwala,ndipo pa radio yabomayomweyo sabisa bwanji?poti nayenso ndi president kwawoko,awa anuwa ndiye kumabisa musaiwale kuti anthu anapenyatsopano,ingothuzani kuti amafuno abwino azimuikiza mmapemphelo,ziwanikuti amalawitu sakumuikitsa mmapemqhelopresident vuto ndiinuyo pomupangitsa kukalangati sakudwala,mukhalendi chitsanzo pamugabe akadwala amawauza anthuawo ndipo amapemphelela mafuno abwino anthu amzikolawolo,ndichifukwa akupezeka alimoyobe mpakanapano,inu zizikuvutani ndikubisakwanuko,mukukhalangati mukumkonda apo simumamukonda

  6. Nonse Ndizisilu Chimene Mukuyiwala Ndicoti M’tsongoleli Amalowa Ndi Voti Ndipo Ali Ndiwomusatila Wake Ndiye Zicilu Mungoti Atule Pansi Mukuwona Ngati Alowapo Ambuyanu Mavuto Sazatha Ngati Cimukupemphera Muku Ngolimbana Ndikudikila Kumwalila Kwazanu Muli Ndisoka Inu

  7. Koma panopa ali kuti? Nanga akupezako bwanji? Kodi papeza athuwa akukamba zambili wena akuti wa mwalila wena akuti amalawi kukonda akazi tikachoka kwathu kupita kwawena sitifuna kupotoloka kodi akulowa chinawavuta ndichiyani?

  8. Kkk Masiku ano , zaphweka! Zokwera, zachuluka “ndi mchaka achule akumaziwa . Chifukwa chilinchonse chikutenga mphavu , komwe kuli achule

  9. sosendizachabe zimenezi ngachitike tizirandire koma akakhara kuti wamwarira tivomerezesikuyamba kuti president afe paribe voto bora atiuze chirungamo chammene ariribasi osatikubisako atakharakutiadafatiyamikirapakutisitikumufuna chifukwadziko ramukanika afe basi tiribenayentchito afe ndithu ife tikondwa basi

  10. àmene ánapangà nyimbo yafuko lathu anqlingalira,dalisani mw “izi njára,nthenda kmanso nsanje apa pansanje mulungu ayikepo dzànja chonde Amen

  11. Àmipingo nthawi ya vote mumapempera kti mavote ayende bwno,vula ikapanda kugwa mumapanga chimozimozi nankuĺu akadwala simutero bwanji ollo titasi ntha kngati siziyande basi mulungu adalinse malawi
    t

  12. WHY CAN’T U TELL D NATION YOURSELF IF U KNOW ALL ABOUT DE PREDIDENT’S HEALTH RATHER THAN FORCING SOMEONE TO RESIGN IF U HAVE D GUTS

  13. Ine ndakwiya heavy
    Had it been kuti anatiuza that my no1. Worker is sick i could have left him in the states kuti alandire treatment yokwanira. Panopa tingoyang,ana patsogolo, not zotula pansi udindozo, president wathu wokonzamiseu uyu.

  14. POOR REASONING DEMONSTRATED. IN A POLITICAL WORLD, LET’S LEARN TO BE CRITICAL WHAT SOME TINGS LIKE WHAT HAPPENED WITH US ARISE. THERE WAS NOTHING WRONG….

  15. Kkkkkkkkkkkkkkk Achisi inu mukadwala amadziwa ndani?Sibwino kukhala ngati anzeru pa vuto la nzanu moto umamka komwe kwasala thengo.

  16. Palibe akubisa matenda aliyese akuziwa kuti munthu akudwala mufuna muonere chani ?osamakadwazika ambuyanu kumudzi kwanu apa muli buzy ndi matenda ayinyake

  17. Don’t make decision for him , if he feel like he is strong enough that he can make it then let hime continue, don’t force him to step down, jst waite 2019 then u will remove him as of now don’t take advantage for his sickness! Rassul Nala Seniour

  18. Ulemu Pa Udindo Wa Azathu Ndiofunika~ Komaso Kuganizila Anthu Ngati Ife Kudziwa Zamtsogoleli Wadziko Alili Ndikofunika~ Utsogoleli Ndidziko Zizikomela Anthu Osati Kuyimitsa Dziko La Anthu Ambili~mbili Kusadziwa Chomwe Chachitika Kwamasi Osewa ~ Tidzakonda Mutakonda Dzikoli

  19. ANACHITA BWINO WOSANENA CHIFUKWA KWACHULUKA MA PROFIT WONGOLOTSERA ZAMATENDA NDI IMFA BASI ZABWINO ZONSE APROFESOR AMBUYE ADZIKUTSOGOLERANI. AMEN

  20. Ambuye che kapito, APM sangatule pansi udindo chifukwa chotulila palibe. Kodi walakwa chani? Asiyeni akunenawo ali ndi zifukwa zawo chisankho chija sichinawathelebe ifetu timaiwala kale pano tikukonzekela 2019 kkkk

  21. Ndizoona president ayenera ulemu koma matenda SITIMABISA!
    Nanga akanafa mukanati chani kumtundu wa a malawi?
    APM NDI MUNTHU WABWINO KOMA MBUZI NGATI NDAU NDIAMENE AMALAKWITSA ATSOGOLERI.
    As a true son of Malawi i stand REBUKING NDAU KUTI ANALAKWITSA AND APEPESE!
    STOP INTIMIDATING PEOPLE KUT MUWAMANGA!.
    NANGA ANTHU AMANAMA THJAT OUR DADDY WAS SICK?
    BULLSHIT!!
    MUNABWELETSA MUNTHU ODWALA ASANAMALIZE TREATMENT WHY
    THE DESTINY OF APM, OUR DADDY IS IN UR HANDS U CABNET MINISTERS!
    THIS IS MALAWI ZOOPSEZANAZO AI!
    KUPUSA!!

  22. No president shall rule forever, kunali achina kamuzu pano sanazisiya. DPP hide infor about the weakining of the president in order to remain in power forever.

  23. Akuteroyo ndi mbuzi ya munthu!!!!!!. President ali ndi ufulu osungiridwa chinsinsi osangoti bola ndi mfumu ya dziko naye ndi munthu….ba nsolo wanu ukuphatabi wasowa cholonga dyabu.

  24. Lets handle this issue seriously..kudwala kwa president sichithu choti chizingolengezedwa..Chabwino kodi anakati akuuzeni kuti Peter akudwala,munakatani? panopa mwaziwa,mutani?? Anthu ena akuti atule udindo..Kodi president akadwala muzitero? Tiyeni tiziyakhula ngati akuluakulu

  25. guyz maganizo akupelekedwa osiyanasiyana fuso mkumati mwapindulanji? musataye nthawi yanu pachabe chifukwa inu ndine tilikutali zedi ndi dziko la malawi pazifukwa izi amatinamiza kumati boma ndi athu zimene sizili zoona kamba kakuti.ife athu timapeleka maganixo abwino ndithu koma saphula kathu. kwa axathu aboma chifukwa safuna kupangiridwa kathu ndi athu amene ali ktali ndi dziko .chenjexo osamataua nthawi kumalimbana ndi boma musafa mukanali ka bee

  26. President ndi kholo la dziko, kodi mungave bwanji m’modzi mwa Makolo anu kudwala mwa Sirius inu osakudziwitsani kwa nthawi yaitali?. Ndikulakwa kubisa matenda amsogoleri wa dziko, ngati alangizi adalamulidwa ndi a president ndekuti ntchito idawalephera.

  27. kkkkkk amene akuteloyo ndi mbuzi yamunthu kodi matenda amalengeza ngati ukwati? Kodi akanalengeza ndi phindulanji limene iwowo amayembekezela kupezapo? Iwo aziwa mmene apresident aliri akufunananso kuuzidwa kuti chani?

  28. ???????????? Childish mind in DPP Cabnet Ministers mnazolowera zaufiti kumidzi ya kwanuko nchifukwa mmabisa matenda a APM , akanauzidwa zoona amalawi kuti Peteryo akudwaladi ndipo akupitiliza kulandila chithandizo ku USA ndikuona kuti Cabnet iyi yili ndimanyazi penapake but ayo ndimatenda there was no need to hide and forcing him come may be u want Peter to die in style as late Bingu iweee NDAU ndimawu ako aja akuti Peter was enjoying robust life in USA ndiwe chisiru choyamba pa azako onse mu Cabnet yanuyo ndiwe Minister wa information watundu wanji ndimaboza akowo

  29. Galu chisi wamva ukufuna MDala yanga isiye ntchito then tizivutika iweyo uzinjoya ndi ana ako mbuzi yamunthu wandinyasa wamva kape!!!!!!!!!!!!!…………

  30. Matenda a head of state sanganenedwe anyhow never , akudwala malungo, ai bwana adwala mutu aaaaa nde si President – tu. Asowa nkhani awa

  31. Achoseni muyikepo aziwana anu, sizomwe mukufuna? Mumafuna achite kulengeza matendao ngat sadaka? Matenda ndee obisdwao maka pamunthu wamkuru ndpo anachitabwino kubisa

  32. Okey mukutukwanisa peter ndiiunu eti, dziko silikuyenda eee mavuto akuchuluka ayiii peter mwakuti mwakuti mukulangaza inuyo iye mkumaipa ok

  33. Palibe zimenezo atule pansi udindo kamba chani amenewa alipo mpaka 2024, ndipo sinaone alangizi anzeru ngati awa , inu matenda anu mumauza ndani?

  34. Poyamba tione kuti malamulo adziko akuti chiyani. Kodi lilipo lamulo loti mstongoleri wa dziko akadwala alengezedwe? Aneneri asiyeni iwo amatsata lamulo lantchito yawo imene analembedwa. Tikudziwa ku enenanu mukufuna achabale anu alamulepo koma adikile 2019

  35. Mzelu zoputsa alibe vice wake?vice timamusakha kuti wapampando akakhala kuti watsamaya kapena wamkalashika.amagwira ntchitozo ndi viceyo

  36. Kodi basi chilichonse chochitika mdziko muno anthu azitula pansi udindo,ntchitozo mugwira ndinu?Nde atula pansi maudindo anthu angati?

  37. Forgive and you shall be forgiven too,not everybody is perfect..love doesn’t keep a record of being wronged 1corinthians13:4-7, for those who believe in Christ ,let’s pray to God for our president and the nation.

  38. mukanatani mukanadziwa?enanu ngakhale kumudzi kwanu mumangovera kuti,auje(ena mwa abale anu )kuti adamwalira,ndipo simunakapepeseko ata,zamatenda olo mutapita simuthandiza kanthu, pano mwaona zili pa ena mwayamba kutumbwa

  39. Kodi munthu tsamadwala? Vuto ndi jealousy lomwe lanyuluka kwa A Malawi olo atatula undidowo enanu tsimugakhale a president.

  40. Zanuzimenezo pamene mumasakha khalambamo ine sanandilamulile nawo adwale asadwale ndilibenazo tchito koma osati mpaka kutulisana udindo

  41. Anthu oipa anthu adyera anthu wosakonda dziko lanu mungosokosa apa ngati za nzeru kuyambira pitarayo ndi nonse atsogoleri andale kuphatikiza inu nomwe wosusanu, kodi mungoti atule atule amene atalamulire akatulayo ndiye ndindani ndiye inu ndamene mutasinthe zithu, mungoti atule cz nanunso mufuna mumomotoremo, mungokharira kuba ndalama za mphawi amzanu maiko akunja akaba choncho amapanga zitukuko mudziko mwawo momwemo kumanga ma company ndikumalemba anthu ntchito pamenepo amakhara waba koma atleast ena akuthandizika nawo, pamene inu mukaba ndipamene mukukakhazikika kunja moti mumange tima company kumeneko kumalemba achinyamata ntchito ayi, enanu mungoti achoke inu ndiye mubwera ndi phindu lanji mwapanga chani chotukura dziko lanu chomwe tingaku sapoteni kuti eya achokedi bola inu,

    1. Bingu anthu ankati achoke achoke koma atachokadi zinasintha, im nt a fan of dpp and i wil never be koma zikutisokosa

  42. Amalawi mwasowa ntchito zoona tsiku ndi siku nkhani ikhale ya mutharika walakwanji?Mpake kuyankhula Nga mtafu anati AGALU INU Mnyumba ya malamuro,ndizoona ndife agaludi.

  43. 2019 mpando umenewu ndikudzautenga basi! Amalawi mwatopadi ndi mavuto. Ndizangobwezeretsa mchimake zomwe zasokonekerazo monga magetsi,madzi,mankhwala mu zipatala,nkhani ya njala ndi zina kenako mkutula pansi udindo chifukwa sumandisangalatsa! Panopa ndili busy ndi ma bungwe akunja kuno kukambirana nao moti tagwirizana. Koma akuti ndidzachepetse ma unduna chifukwa ndi omwe amasokoneza president.

  44. Kodi Mukumutenga ngati president munthu Wamba ngati inuyo ndi ine ??chomwe mungaziwe ndichakuti even atati wamwalira palibe amene angakuuzeni pa tsiku lomwero iyi imakhala mbali imodzi ya Security mudziko…Ndizandaletu izi

    1. #Roosevelt sindingafotokoze kwambiri chifukwa #Eneya Banda wanena kale. Ndipo usakaike kalikose pa izi zimachitika ndinthu. Sindikudziwa kuti moyo wachikale ukunenawo ndiutiowo ?

    2. Inu chifukwa pamakhala vice wake security yachani mukunena inu koma umbuli ndivuto lalikulu etii kkkk.taonapo president kumwalila vice kupitiliza chimozimozi akachoka vice amagwirizira…kukhala kuononga ndalama zaboma si izi akuononga kale kkkkkk umbuli amalawi ukutipangisa uchitsiru

    3. Inu #Akumwenda inuyo mzeru zanu zili pati? Ndindani samadziwa Kuti mtsogoleri aliyese amakhala ndi womutsatira wake????? Inu simukutha Kuona kusokonekera kwazinthu pakanthawi komwe mtsogoleri wanthu wadwalaka???

  45. Koma anthu inu mukufuna kut anthu atule pasi maudindo awo ndikulakwa kwbiri ngankhale mukusintha chingachitike ndi chn mmmnmn muziganiza aMalawi musanapange discus oky

  46. Ngati anamupasa ok kuti aziwise ntundu wa Malawi nde sanatero akagwere uko koma ngati sanalandire ok then it’s not his fault olakwa ndi aprensindent wo.

  47. Nanga mchifukwa chani malilo awanthu ngati amenewa amawayendesa ngati kanema apange monga amachitila malilo matendaso choncho,

  48. Ndili ndi nkhawa mmoyo mwanga, anthu dzulo andiona ndikupereka moni ndi mkono wa manzere. nkhawa yanga ndiyakuti safalitsa kuti ndikudwala pamenepa shaaaa

  49. ngati atagwilizane nazo zotula pansi udindowo.ineyo l think l can do that job better than anyone else by the help of my Lord Jesus just as Joseph did advice potipher

  50. Kuti muonesese alangiziwo are just for show, they were in the dark as we were, i think in the government machinery only chaponda new what was really going on.

  51. Ine ndikamakhalatu ndimaona ngati mtsogoleri wadziko akadwala kwakanthawi, boma limayenera kuuza dziko chifukwa kudwala kwa mtsogoleri kumapanga affect aliyense through economy

  52. ACCESS TO INFORMATION BILL could give us a chance to give us an opportunity to know everything concerning our president’s health too. bisani matenda, maliro tidzamvera pa ZBS kkkkkk

  53. For The Security It Is Not Allowed To Broadcasting When A President Is Suffering Or Injured.Only A Death But It Also Take For Some Days So Thats A Palatble To Sack Them For Those Who Mulling Oversomething.

  54. Akunama musatule ndkunena ndne Eno Kadzuwa,, munachta bwino kubisa cz kuno kwachuluka afit nde akanangoziwa kut akudwala akanatilodzera Presdent wathuyi

    1. Koma nde afitiwo sasakha kkkk.. nyama yake nde aaaah…kukhala kalulu nde okalamba sadibwa, kapena ng’ombe ..nde yokalamba chocho ingakome? Kkkkk palipose muswididi kkkkk

    1. Wopusa 100% ndiwe chifukwa walowetsapo tribalisim & regionalism.kodi akutchula za Peter ndi mtumbuka? kodi atumbutufe tili ku Zambiya? Samalani pakamwa mani.

  55. ….. akatula ndiye alembedwe iwo..? It’s our traditional and culture kuti munthu wamkulu akadwala kapena kumwalira, sitimangoima pachulu nkumaimba chiminingo ngati kwaphya mowa wamasese….!! Kale mfumu ikamwalira achule sankadziwa……

    1. Munthu wankulu landirani ulemu wanu kumeneko ndiye kulankhula.Sizowona kufalitsa mwatenda a munthu wankulu ayi boza lenileni.Ime ndikupempherera kuti asamwalirenso anrhu akufuna koyopa amaunena kwabasi.Akamwalira ndiye nyanyee koma mulungu ansunge achita kale kwakukulu.Munthu uu sakanabwera ndimaganza kuti wamwalirabasi Mmene anthu amalankhulira

    2. koma ukudziwa kutukwanika kosekuja amatukwanidwa APM ndichifukwa cha ndale za manyi za ena mwa a DPP anaonjexa masiku kunja alangizi akanati safika msanga akulandila thandizo kapena wayamba Holiday sizikanafika apa komano anthu anadziwa kuchokela komko kuti alowa mchipatala kufusa kuti adziwe moyo wa mtsogoleri wao mmalo moti eya koma pano akupezako bwino mkumalana akuti akugwila ntchito zina chikhalilecho panalibe chochita choonjezela Ndani sadwala oyamba ndiye kapena iye ni Mngelo changamukani a Malawi

    3. Uthenga wa imfa ndi matenda. Ngakhare buku lopatulika lidaima ndi chichewa kuti “WOBISA MACHIMO AKE SADZAONA MWAI,KOMA WAKUULURA NDI KULAPA ADZACHITIRIDWA CHIFUNDO” choncho alangizi a president ali ndi vuto komanso DYERA. Ngati akuuzidwa kutura pansi udindo,achite zomwezo.

    4. Zobisa matenda kaya imfa zakalekale…chifukwa dziko lathu ndilosalila…nanga kuti tikhale ndi anthu 100 anzeru ngati bambo SIMON BARLE ziko lingatukuke? Akunena zakalekale thawi yoti kukachitika malilo ana onse amasekerdwa nyumba kkk zinasitha pano tili mu democrancy babaaaaa!

    5. munthu wamkulu landirani ulemu,enawa kulankhula konseko ndi ndale basi,amafuna udindo ,kapena amafuna munthu wa chipani chawo atenge udindo

    6. No president shall rule forever, kunali achina kamuzu pano sanazisiya. DPP hide infor about the weakening of the president in order to remain in power forever.zosiyilana izi

    7. mr Simon Barley this is a democratic country, where information is a right of every citizen. sometimes i question if we really are in a democratic country or not.

    8. Zili apa si zandale ko chilungamo chitsatidwe bansi kodi tidzakhala mu mdima mpaka liti ? Iye ndi tate wa Malawi n tayenera kudziwa zonse pompanda chinsinsi.Funso kwa enanu mungasangalala bambo anu akudwala kwambiri nde anthu akubisileni matendawo?

  56. Munthu aliyense amadwala chifukwa awa ndi matupi. Kodi ndiye kuti akunenedwayo iye sangadwale? Nanga nkono uja chinali chani, mwina inali American swagga? Vomeredzani basi anthu opemphera azimuyika mumapemphero.

  57. Koma Anthu Pali Khaniso Apa Mumafuna Adzichita Kulengeza Zamatenda Ngat Ndi Ukwat Akatsengula Mimba Mudziwe Bas Kodi Inu Muli Bwino Dzisungilen Ulemu

  58. Koma mpaka kubisa matenda? Atsogoleri oipa inu , akanakhala kuti ndi Bambo anu kapene achimwene anu mukanabisa? Kunena chilungamo ndikwabwino cause anthu ena omufunira zabwino atha kumamuikiza mmapemhero

    1. Inu mukuona ngat mavuto tkuwaona ifewa maiko aza2 sakuona zomwez khalani tcheru nthw yafka mulungu aweruze. Ma respect ma APM.

  59. happu am the 1st to comment i would like to thank my mom my dad and my wife i couldnt have done this without you……i love u

    1. Changu pamalo what a platform even bible limate Lemekeza atate ako ndi amako kuti masiku akoachuluke m’diko limene Yehova Mulungu wako anakupatsaa.#one must fall.

Comments are closed.