Kongeresi? Ayi ndithu mwanawe, ndinali komko paja – Dausi

Advertisement
Dausi

Ati muziliyatsa la mtondo wadooka mukangomva za tambala wakuda. Ati pali Kongeresi, a Malawi nonse muzipita kukabisala ndithu osati kuthamangilako.

A Nicolas Dausi amene ndi nduna yoona zofalitsa mauthenga komanso mneneri wa boma anauza msonkhano ku Mpherembe mu boma la Mzimba kuti chipani cha Kongeresi sichosewela nacho.

Nicholas Dausi
A Dausi akuti Kongeresi si chipani chomachiyikila kumtima.

Pa msonkhanowo umene anachititsa ndi a Peter Mutharika, a Dausi anati Kongeresi simalabadila lonse anthu a kumpoto.

“Inetu paja ndinali komko ndinachita chothawa. A Malawi, Kongeresi si chipani chomachiyikila kumtima. Tsankho ndiye kudya kwawo,” anatelo a Dausi.

A Dausi anaonjezelapo kuti mu masiku a Kamuzu, ma unduna a zachuma ndi ntchito sakanaloledwa kuti apite kwa munthu ochokela ku mpoto kamba ka tsankho.

“Koma taonani lero, a nduna a zachuma ndi a Goodall Gondwe pamene a Jappie Mhango ndi a nduna a zantchito,” anatelo a Dausi.

Polankhulapo a Gavanala a DPP a ku chigawo cha kumpoto a Kenneth Sanga anati chipani cha DPP chisesa mipando yonse ya uphungu mu boma la Mzimba kamba koti anthu ndi okondwa nacho chipanichi.

Advertisement

2 Comments

  1. Anthu akumpoto ndiwo atsango latadzaonani osati Malawi Congress akunama

Comments are closed.