Chipasupasu ku Manoma: Kamwendo azitaya, timu imukakamila

Advertisement
Joseph Kamwendo

Ululu wa Vita ukuzunguzabe Manoma. Mbwiza anavina Manoma ku Congo, Tchopa wa pa Bingu adakawazunguzabe a ku banja la nyerere. Inu, Vita si zibwana iyayi. Ndi izi lero Manoma ali ngati pa nsanja ya Babulo aliyense angolubwalubwa ngati oduka mutu.

Patangopita ka nthawi kochepa, Esau Kanyenda atalengeza kuti wazitaya ku Manoma, tsopano naye Joseph Kamwendo ati wazitaya naye.

Joseph Kamwendo
Joseph Kamwendo

Sabatayi yayamba mowawasa ku Manoma pamene zinaululika kuti Kamwendo amatafulila anthu ena mu timuyo kuphatikizapo a Esau Kanyenda kuti akufuna kumulanda u captain.

Izi zitachitika, Kanyenda analengeza kuti wazisiya ku Manoma. Lingaliro lake linagawa pakati anthu okonda Manoma pamene ena amaona kuti kuli kwabwino iye apite ndipo ena amaona kuti Kamwendo ndiye olakwa.

Dzulo lachitatu, Manoma analengeza kuti Kamwendo amuvula u Captain. Sipanatenge nthawi, naye Kamwendo analengeza kuti wazidomoka.

Koma wapampando wa Noma, a Gift Mkandawire wati Kamwendo samulola kupita iyayi.

Poyankhula pa wailesi, iwo ati Kamwendo ali ndi contract yofika chaka chamawa adakali ku Noma.

 

Advertisement

68 Comments

  1. Sizikugwirizana ndi za ma game aku caf, inuyo si ma reporter abwino mmalo mowaziwisa anthu bwinobwino zikuoneka ngat kut ndinu aganyu mmene mwalembalanu mwina zikukusangalaniso kut kuli mpungwepungwe Ku manoma. Mwalemba ngati kut mukupanga comment. Mmxxxxiee ma reporter opusa

  2. komano neba uzikhalako ndi manyazi zigolo zonse zija ifeyo tizingochemerera poti ndiwe wakuno ayi sitipanga bola malo mwa inu kukanapita blantyre united

  3. Ndiye Kuchemelera Vita Chonchi Ngat Ndiwe Waku Drc Bwa? Wapenga Kapena? Mzikhala Ndichikondi Ndizinthu Zakwanu Mbuzi.!

  4. Ndiye Kuchemelera Vita Chonchi Ngat Ndiwe Waku Drc Bwa? Wapenga Kapena? Mzikhala Ndichikondi Ndizinthu Zakwanu Mbuzi.!

  5. is this page for bullets fanz ? tell me pple , I might be at a wrong page . I don’t blame yu Mr admin , but this cud’ve been avoided abambo ako akanagwilisa ntchito condom

  6. Manoma Can U Write Report Zamomwe Mudayendela Mu Cuf Paja Zinali Zigoli Zingati Pamodzi Kkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkkk

  7. Ngakhale zavuta ku-nomako koma amene walemba nkhaniyi nayenso zikumuvuta kulongosola bwino and akapitiliza kulemba zosalongosoka azaononga page ya #malawi24….

  8. Ngati Bullets inapha Pirates,African sport yaku ivory coast Vita ndikachani kwa BB ukaifunse Zanaco mpaka kufika mateam 8 otsala the whole Africa mbiri tinapanga kale ndi chifukwa maplayer anthu savuta msika kkkkkkkkkkkkkkkkk neba

  9. Kodi basi mwangopeza nkhani, koma muchita manyazi ose atabwelera ku banja la noma coz ose alindima cobtract omwe akuchita run till 2019.

  10. NOMA SUPPORTERS KUZALUSA PAMENE PAJA KKKKKK
    UBWINO WAKE MWAIYETSA CAF, NDIYE YAKUOTCHANI MANJA…
    IFE MZUNI FC GONKOKO 2018 MOTO KUTI BBUUUUUU… BOMA ILOO.
    WENGER OUT!!!!

  11. Things fall apart- mano. by okoma atani malunga.
    Malangizo munapatsidwa koma kusamva.Mubweze ndalama kwa sponsor wanu nbb.

  12. INU AMALAWI 24 VITA SIYAKU CONGO KOMASO ZOMWE MWALEMBAZO ZIKUONETSA KT KULIBE ANTHU OPHUZILA BWINO AND MUPEZE CHINA CHOCHITA OSAMATINAMIZA NAFESO ZAMPILA TIMAZITSATA

  13. Nkhani yanu mwayikamba mopusa mosayenera mwawumburi chomwe mukanalingalira choyamba ndi kuwuza anthu mobveka bwino bwino kuti azindikire zomwe zikuchitika Ku wanderers osati mtopora mwapanga apawu ayi

  14. Iweyo admin, football club imene umasapota m’Malawi muno ingagonjetse Vita? Ndakuonatu ukulemba nkhaniyi motumbwa. Nkutheka umasapota team ija ya neba ija. Kkkkkkkk bola nyerere, of course zinavina mbwiza komabe, zinatichotsa manyazi coz they qualified for the cup. Nanga iwe admin ndi team yakoyo mwapanga chiyani cha nzeru chaka chino? Kugonjetsa Karonga United basi?

    1. inu mwapanga qualified cup yanji ,mwatuluka muma early stages ya caf ,pali cha zeru pamenepo Kklkkkkkkkkkkkkkkkkkk zobeba izi kuzimva bwanji

    2. Kkkkkk akufuna atiuze kt chazeru ndikupanga qualified basi not kuwina analibedi cholinga chencheni chomenyela caf makapewa

    3. Unakadziwa Ching’amba,sunakalemba zalubwalubwa zakozi,ng’ombe zayang’ana ngolobasi kwasala nkuvomereza.mukalimbana ndiife muthawa

Comments are closed.