‘Kulidi katangale kuno?’ boma la a Mutharika likukayika


Money currency

Zonse zija zoti a Malawi ochuluka akunyema pamseu, zoti akunyema pofuna ziphaso zoyendela (passport) ngakhale za u dalayiva, Boma la Malawi likukayika zoti kuli katangale.

Mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika amene nduna yawo ya za malimidwe yakale a George Chaponda anachotsedwa pa udindo powaganizila kuti amafuna kuchita za katangale, lero akhala akutsegulila msonkhano wofuna kudziwa ngati zili zoona zoti mu dziko muno muli katangale.

Msonkhanowu ukuchitikila mu mzinda wa Lilongwe. Bungwe lothetsa mchitidwe wa katangale mu dziko muno la ACB mogwilizana ndi unduna wa za Chilungamo ndiwo akonza msonkhano umenewu.

Malinga ndi uthenga ochoka ku boma, ati msonkhano umenewu ukufuna kutsimikiza ngati katangale akuchitikadi mu dziko muno kapena anthu angokokomeza.

Pa msonkhano umenewu umene anthu ena audzudzula kuti ndi chibwana chabe, aitana namandwa wa mu dziko la Kenya kuti azayankhulepo.

101 thoughts on “‘Kulidi katangale kuno?’ boma la a Mutharika likukayika

  1. iiiiiiiiiii Apulezdent Maine nde Salimumalawitu kikkkkkkk Atumize Ma Cid Akaona Xoopsya muma department ambiri Aboma ……ndipo Azakhumudwa………………..vuto Ma cid akalandilaponso ka chiphuphugate koma kaya tilowela kuti kikkkkkkkk…

  2. Katangale sazatha aliopobe zaka zikubwerazi ndiye mavuto osaneneka. Tangopitani ku e migration kuli mavuto osaneneka

  3. Kuipa koika anthu obwera mmaudindo ndkumeneko,,zoona kt katangale kulibe..? Zitsiru…

  4. Ilili Boma Ndilanyasi Ndiboma Losaganizira Anthu Akumudzi Zaka Ziwiri Zathutsa Koma Palibepo Mlimi Yemwe Akusasangalala,boma Ili Lilipo Ndidyera Basi Katangale Thoo!Bolaso Boma La Bingu Komaso Joice Alimi Timakhala Ndi Ndalama Anthu Amagulaso Galimoto Koma Pano Tsopano Chino Chaka Ndichachitatu Koma Opanda Chochitika.Ulimi Sukuyenda Ndibwinoso Programme Ya Subside Athetse Yalowa Ndale Akupindula Sialimi Koma Andale Makoponi Awiri Pafumu Sichipongwe Chimenechi?Ndiye Mkumati Boma Langa Lili Bwino.Chipongwe Basi Especially Kasungu Santhe Sitimudziwa Nkhope Yake Pulesident Ongowina Sayerekeza Kudzawona Mavuto Awanthu Kuno Tsankho Lokhalokha.Ndiye Mkumakana Kulibe Tsankho Ayi Ndithu Ili Siboma Lokomera Anthu Akumudzi Komwa Mwina Amtown.Mlimi Kwake Ndikulira Basi Ngati Sasitha Ngati 2019 Adzawine Adzandifuse Sangawine Olo Mwana Sangakambe Zabwino.Subside Athe Mkwabwino Angochepetsa Mulingo Wogulira Fertilizer Komaso Makalabu Basi.

  5. Kodi KATANGALE ndi chiyani?. Katangale ndi kupeza ndalama kapena zinthu kwa antchito kuchokera kwa anthu adyera kapena opanda zodziyenereza kupeza chomwe akuchifuna mosayenera. Kodi katangaleyu amachitikira kuti?. Katangale akuchitikira m’maofesi onse a Boma, M’mabungwe onse amene saali a boma, M’mpingo ndi monse moyendetsedwa ndi anthu olembedwa antchito. Kodi kuthana ndi katangale nkotheka?. Ine ndikuti AYI, chifukwa ofuna zinthu m’njira zoyenerazi alipo miyanda miyanda ndipo a m’maudindo ngakhale atalandira malipiro ochuluka bwanji, sadzatheka chifukwa katangale wa chaka chimodzi akutha kupanga zomwe sadakatha m’zaka makumi awiri. Mutapita kwa ma MP anthu onse chiyambire 1994 mukapange kafukufuku mukapeza kuti chuma, ziphaso zoyendetsera Galimoto, zilolezo za mabizinesi anazipeza kudzera m’katangale kapena kuba kumene ndalama zoyambitsira bizinesi zao. A ACB, M’mabungwe omwe siaboma, M’mipingo ndimwina monse muli anthu pafupi onse amenenso angayankhepo milandu ya katangale kapena kuba ndalama kumene.

  6. Kkkkkkkk koma mkuluyu mutu wakwe ukugwira ntchito? Si yekha pompano amanena zoti akudziwa kuti boma lake katangale alimo koma achita chotheka kuti athane ndi aliyense okhuzidwa nde pano akufunsaso?

  7. Umeneo ndio timautcha uchisilu a Malawi, ndani asakudziwa zoti Ku Malawi kuli Katangale, ACB nao linangokhala dzina pano, Kuba kuli nkati…..

    zopusaa, mkaitane munthu Ku Kenya kamba ka Nkhani yakatangalee?

    Malawi dziko langa likumvetsa chisoni…….

    izingodyani Ndalama zoo mlemele ndinuuu

  8. Thats y ifeyo sitizasiya kutukwana pa fb cz boma ili ndi lankhutukumve zokhazokha ndichifukwa chan mukulesa zinthu zoti ife tikuvutikanazo abakha inu mbuzi za an2.

  9. They know each n every corner do u think that they should say yes there is corruption in our gov even u, u can’t say yes while u know the truth go to traffic or immigration

  10. Uthenga opita kwa ma cadet nonse @DPP kuikira kumbuyo zinthu zoti pansi pamtima mukudziwa kuti zolakwika komanso zikuzunza fuko lamalawi ndi tsoka!!
    Pali nkhani zoikira kumbuyo Boma apa?

  11. mmmmm Malawi Malawi my country,what kind of leadership is this? u think we dont know what is happening eshie nanga ndalama zija boma linalipira magalimoto kuchoka ku SA zinayenda bwanji mumalo mwamagalimoto 8 kubwera atatu five missing eshie

    1. So you are comparing Malawi & some countries? Maiko ambiri omwe kuli katangale anatukuka kale ndipo amakhala moyo otsogola.kkkkkk ukukamba ngati chifukwa chakuti Ku Russia Ku li katangale ndiye ife tizipanga katangale. Waiwala kuti maiko amaneo anatukuka kalekale ndipo anthu sakhala mu umphawi ngati Ku Malawi.

    2. U mean tizingoba popeza tili mmasiku otsiliza? Tiyen ngakhale tili mmasiku otsiliza tikonde dziko lathu coz palibe yemwe akudziwa tsiku lenilen mwina kwasala zaka 100 kutsogoloku

    3. Malawi is worst corrupt country in the world as well as poorest country. Don’t compare it with other developed nation in the world

    4. Ok watelo nanga … What f ur brother hv a head chopped-off and u catches a guy who did it…and the guy got alot of cash and he agreed not put in jail coz he bribed wil u say its gud………. B’ generous….. Corruption its not political only my friend……… Some of us we hv faced unlawful judgments due to corruption” this should come to an endnow am in USA this month its not like Wat z there at home

    5. Tony phiri, U.S.A and malawi is different, there’s corruption in U.S but u don’t know coz is developed country, and even here in Britain, people r singing the same song, but we poor we don’t know, so don’t expect malawi to change, kamuzu never develop malawi and no one will develop malawi.

  12. A Peoples Party Anatuluka Ndi Cashgate! Adpp Maizegate! Ndiye Bola App Bcz Anthu Ntchito Ankalembedwa Ndalamaso Zimalowa Kuchoka Kunja Ambiri Anthu Anapeza Nchito Muma Department Osiyanasiyana Pano Kuba Kokha Opandanso Manyani! . Sindine Wachipani Koma Zabwino Zoyipa Timaona!

  13. Ndani Angavomeleze Zochititsa Manyazizo?Palibe But The Truth Z Mw Z On #1 Corruption.Mukanena Zapamseu Apolisi Ndiye Siyani,tifunseni Ife Timauser Public Transportfe.Eeesh!Nyaaansi Pamseu

  14. Sangavomele ayiwala kale kuti nduna yawo (Chaponda)adayichotsa poyiganizila zakatangale? Timapenya maso tilinawo komaso timava makutu tilinawo simungatinamize sindife ana.

  15. Boma ngati silikuziwa za ma department ake zomwe zikuchika nde kuti ali ndi chidwi ndi anthu ake??? Ulamulilo wa DPP ndiplephela.

  16. Vuto katangare sadayambe ndi boma lake lilipoli ayi adamba ulamulira wa Bakili komaso ngat ukuchifuna mwachangu chinthu uyenera kunyema basi.

    1. Meaning DPP/UDF Collision it’s major agenda if to promote tactics of Corruption backed by Corrupt leaders with their savages the so called Cadets/Young Democrats? Manyaka a BOMA awa!!!!

  17. Aluza 2019 chifukwa chainu koma ine nditamvotera osatha zamkamwa sindiona president wina mmalawi muno mwina povota kapena pa campaign pano iye bas nde tiyeni tidikile 2019 mukukhala ngat osazindikila bwanj president nde angatule udindo chifukwa chomunena remember president sachosedwa ngat zino koma inu ayi mukundi………ZAMKUTU

    1. Oooooo Ndakuyamikilani kwambiri chifukwa cha ndemanga yanu mwene ndipo ndiyogwira ntima kothelatu zimenezi amene amazidziwa ndi ochepa kunena zowona

Comments are closed.

Discover more from Malawi 24

Subscribe now to keep reading and get access to the full archive.

Continue reading