Wayamba kampeni Mutharika, ali pa Njamba mawa lino

Advertisement

Mtsogoleri wa chipani cha DPP, a Peter Mutharika amene owakonda amangoti APM, akuyembekezereka kugwedeza mzinda wa Blantyre mawa lino pa 12 May. A Mutharika amene akhala nthawi osachititsa msonkhano wandale alengeza kuti akhala pa Njamba Freedom Park.

Malinga ndi tsamba lawo la Facebook, iwo ati akubwera pa Njamba kuti afotokozere a Malawi mfundo zawo za chitukuko maka pano pamene alengeza kuti ayimanso.

Msonkhano wa a Mutharika ukubwera pamene kwabwera chipani china chatsopano cha PDP chomwe akutsogolera ndi a Kondwani Nankhumwa omwe anathamangitsidwa mu chipani cha DPP. A Nankhumwa adati akhala akuchita misonkhano m’madera osiyanasiyana mu dziko muno kukhazikitsa chipani chawo. Ena akuyesa kuti a Mutharika akuchititsa msonkhano wawo pofuna kukhala patsogolo.

A Mutharika, amene amakhala ku Mangochi, alengeza kuti ali ku Blantyre kukonzekera msonkhano wawo umene autchula kuti mega rally.

Advertisement