“Tangowapatsa zigoli” watero Ikwanga pomwe Chitipa yafa kwa Wanderers yomwe yapita pamwamba
Mphunzitsi wa Chitipa United Kondwa Ikwanga wawonetsa kusakondwa ndimmene timu yake imatchingira kumbuyo pomwe timu yake yagonja ndizigoli zinayi kwa chilowere mmasewero omwe anachitikira pa bwalo la zamasewero la Chitipa mu FDH Premiership.
Isaac Kaliati, Lameck Mithi ndi Muhammad Sulumba komaso Blessings Joseph chodzibaya yekha, anathandiza Manoma kuti adzibwerera ku Blantyre ndi chipambano.
Atatha masewero, Ikwanga anati: “Zomwe tinakonza kuti tisachinyitse mphindi khumi zoyamba sibwezi titagonja chomchi. Zigoli tachinyitsa anyamata kumangoonera, zigoli zongopereka.”

Komabe Ikwanga anati zomwe zachitikazi ndizomwe zimakhala m’masewero a mpira ndipo wati akawayankhula osewera ake poti ndi ana.
Chitipa United ili pa nambala 13 mu ndandanda wamatimu pomwe yapeza ma point 6 mmaseweroso 6.
Kumbali yake, m’phunzitsi wa Mighty Wanderers, Bob Mpinganjira, anayamika osewera ake popeza chipambano chazigoli zambiri, ngakhale anati sanali masewero ophweka.
Zateremu Manoma apita pamwamba pa matimu onse mu mpikisanowu atasewera masewero 6 tsopano ali ndi mapoint 13 ndipo achotsa Silver Strikers pamwamba yomwe akufanana nayo ma point koma Wanderers ili ndi zigoli zambiri.









