Tiloreni tizimenya onse onyoza inu – a Ntaba apempha a Chakwera


Lazarus Chakwera

Ati ngati mukunyoza a Chakwera mukufunika kumenyedwa, ndipo bambo Hetherwick Ntaba amene mmbuyomu anatchulidwapo kuti akudziwapo kanthu pa nkhani zokupha anthu a chi alubino azipereka kuti azithana ndi nonse onyoza a Chakwera.

Nkhalakale pa ndale a Hetherwick Ntaba wapempha mtsogoleri wa dziko lino kuti awalole iwo ndi anthu ena kutsina anthu onse onyoza a Chakwera. Poyankhula pa misonkhano yongoimaima yomwe akumachititsa a Chakwera mu chigawo chapakati, a Ntaba anadandaula kuti a Malawi ena akunyoza a Chakwera.

“Bwana, anthu akukuonani kufatsa bwana ndiye akumakunyozani bwana,” iwo anadandaula chotero. “Koma mukudziwa muli ndi achinyamata, ena ndi ife pano ometa pakati.”

Iwo anapitiriza kunena kuti a Chakwera awapatse chilolezo choti azipita kukamenya anthu onse onyozawa.

“Pano tikuti mutisiyire ife achinyamata anu kuti tikathane nawo anthu amenewa, tikawatsine,” anatero a Ntaba.

Sponsored

M’mene amayankhula izi ndiye kuti a Chakwera ndi mayi a kunyumba kwawo ali mu galimoto la mpandadenga akusekelera.

Mmbuyomu a Ntaba anatchulidwapo kuti akukhudzidwa ndi imfa za anthu a chi alubino mu dziko muno. Anthu ena adakhala akunena kuti mkuluyu ndi mmodzi mwa akuluakulu a ndale amene amasowetsa anthuwa kuti akawachitire zizimba.

Discover more from Malawi24

Subscribe now to keep reading and get access to the full archive.

Continue reading