Mtalimanja sanatule pansi udindo, yatelo MEC

Advertisement
Mtalimanja

Bungwe loyendetsa zisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) lati wapampando wa bungweli a Annabel Mtalimanja sanatule pansi udindo ngati wapampando.

Malingana ndi mneneli wa bungweli, Sangwani Mwafulirwa, wati anthu ena akufalitsa uthenga wa bodza kuti a Mtalimanja atula pansi udindo. Iwo ati wapampandoyu akugwirabe ntchito zake monga wa pampando malingana ndi malamulo.

A Mwafulirwa atsindika kuti mu nyengo ino yomwe dziko likuyandikira kupita ku masankho, kupeka kapena kusinjilira uthenga wabodza kumasokoneza anthu komanso ndondomeko ya chisankho.

Izi zikudza pomwe pamasamba a mchezo payenda nkhani yoti wapampando wa bungweli a Annabel Mtalimanja wapita kukatula kalata kwa mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera yotula pansi udindo.

Magulu ambiri ndi mabungwe ena mdziko muno akhala akulankhulapo ndi kufuna kuti wapampando wa MEC atule pansi udindo wake.

Advertisement

Leave a CommentCancel reply

This site uses Akismet to reduce spam. Learn how your comment data is processed.