Mtalimanja sanatule pansi udindo, yatelo MEC


Mtalimanja

Bungwe loyendetsa zisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) lati wapampando wa bungweli a Annabel Mtalimanja sanatule pansi udindo ngati wapampando.

Malingana ndi mneneli wa bungweli, Sangwani Mwafulirwa, wati anthu ena akufalitsa uthenga wa bodza kuti a Mtalimanja atula pansi udindo. Iwo ati wapampandoyu akugwirabe ntchito zake monga wa pampando malingana ndi malamulo.

A Mwafulirwa atsindika kuti mu nyengo ino yomwe dziko likuyandikira kupita ku masankho, kupeka kapena kusinjilira uthenga wabodza kumasokoneza anthu komanso ndondomeko ya chisankho.

Izi zikudza pomwe pamasamba a mchezo payenda nkhani yoti wapampando wa bungweli a Annabel Mtalimanja wapita kukatula kalata kwa mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera yotula pansi udindo.

Magulu ambiri ndi mabungwe ena mdziko muno akhala akulankhulapo ndi kufuna kuti wapampando wa MEC atule pansi udindo wake.

Discover more from Malawi24

Subscribe now to keep reading and get access to the full archive.

Continue reading