Flames yafika ku South Africa kukonzekera chibweleza

Advertisement
Flames vs Southafrica - CHAN

Timu ya dziko lino ya mpira wamiyendo ya ‘The Flames’ yafika mu mzinda wa Pretoria m’dziko la South Africa kukonzekera kubwerezana ndi timu ya dzikolo ya Bafana Bafana Lamulungu lino mu masewelo a mu mpikisano wa CHAN.

Flames yanyamuka lero ku m’mawaku kudzera pa bwalo la ndege la Kamuzu mu mzinda wa Lilongwe ndi osewera 21.

Malawi ikupita pa bwalo la Loftus Lamulungu lino koma ikutsogola kale 1-0 chigoli chomwe chinabwera m’masewelo oyamba pa bwalo la Bingu mu mzinda wa Lilongwe kudzera kwa Zeliat Nkhoma pa mphindi ya chi 87. M’masewelo a Lamungu Malawi idzangofunika kufananitsa mphamvu kapena kupambana kuti ipitilire

Mphunzitsi wa Flames Kalisto Pasuwa anauza atolankhani asananyamuke kuti iwo sakupita kuti akangotchinjiriza chigoli chomwe anapeza koma kukalimbikira kupambana potengera kuti nayo Bafana Bafana ndi timu yabwino.

Pasuwa wati nkhondo inangoyamba pa Bingu ndipo kwatsala ndi kumalizitsa posatengeka ndi chipambano cha m’masewelo oyamba.

Zadziwika kuti mphunzitsi wa South Africa Molefi Ntseki wawonjezera anyamata ake okwana asanu ndi m’modzi omwe masewelo oyamba sanawoneke chifukwa pa tsikulo kunalinso masewelo a mphamvu a SOWETO Derby pakati pa Kaizer Chiefs ndi Orlando Pirates.

Koma osewera onse amene watenga Pasuwa mndandanda uli motele;

GOALKEEPERS
Richard Chimbamba
George Chikooka

DEFENDERS
Macdonald Lameck
Nixon Mwase
Maxwell Paipi
Emmanuel Nyirenda
Andrew Jovinala
Alick Lungu

MIDFIELDERS
Yankho Singo
Lloyd Aaron
Chawanangwa Gumbo
Wongani Lungu
Charles Nkhoma
Blessings Singini

ATTACKERS
Zeliat Nkhoma
Olson Kanjira
Binwell Katinji
Wisdom Mpinganjira
Gaddie Chirwa
Promise Kamwendo
Chikumbutso Salima.

Advertisement

Leave a CommentCancel reply

This site uses Akismet to reduce spam. Learn how your comment data is processed.