ACB yakhazikitsa bukhu


ACB and Ministry of Education have released a book for primary schools

Bungwe lothana ndi katangale la Anti-Corruption Bureau lakhazikitsa bukhu la tsopano lotchedwa “Anti-Corruption Source Book” lomwe lidzigwilisidwa ntchito ndi aphunzitsi a kupulaimale.

Bukhuli lomwe alikhazikitsa dzulo ku Lilongwe cholinga chake ndi kuphunzitsa chikhalidwe, umunthu komanso mzimu wa kulimbikira pakati pa ana m’dziko muno.

Oyang’anila ntchito ku bungweli a Martha Chizuma, anati, bukhuli lithandiza kubwelesa m’bado watsopano opanda chinyengo.

Mu mau ake, mlembi ku unduna wa maphunziro a Chikondano Mussa, anati, undunawu ukuunikaso maphunziro a dziko lino ndipo kuti ma uthenga okhudza kuthana ndi katangale azaikidwa m’maphunziro ena.

Bukhuli Anti-Corruption Source Book lakhadzikitsidwa pa mutu oti Maphunziro Umunthu ndi cholinga chothana ndi katangale.

Sponsored

Olemba Andrew Salima

Sponsored

Discover more from Malawi24

Subscribe now to keep reading and get access to the full archive.

Continue reading