Adad ayenda choduduluza ngati yakwa Manje

Advertisement

Mwakhala mukuona momwe ayendera magalimoto akwa Manje kapena malore otuta njerwa ndi mchenga omwe sitati yake imakhala yoduduluza buleki n’chikang’a.

Umu ndi momwe anayendera a Pulofesa a Peter Mutharika omwe owanyadira amati adad popanga kampeni.

Vidiyo yomwe ikugawidwa kwambiri pa masamba a mchezo ikuonetsa apolisi akukankha galimoto ya bode yomwe a Mutharika anakwera.

Pamenepa nkuti a Mutharikawo atangokhala pa mpando ku bodeko paulendo wawo ocheza ndi anthu dzulo.

Paulondewu, a Mutharika anachoka ku nyumba ya Sanjika ku Blantyre kuima pa Lunzu, pa Ntcheu boma komanso pa Biwi mu mzinda wa Lilongwe.

Polankhula ndi anthu kwa Biwi, a Mutharika anapempha a Malawi kuti azawavotere pa chisankho cha pa 23 June ndipo iwo adzaonetsetsa kuti Malawi atukukuke ndikumaoneka ngati dziko la Amerika.

Mawa a Mutharika akhala akuchoka ku Lilongwe kukapangaso kampeni ku Kasungu, ku Mzimba ndi ku Mzuzu.

 

 

Advertisement