A Muluzi asusula chilonda


Protesters carry banner demanding K1.7 billion from Muluzi- Malawi24

Ochita ziwonesero ndikusakondwa kwa zotsatira za chisankho cha pa 21 May, awonetsa mkwiyo wawo kwa mtsogoleri wakale wa dziko la Malawi a Bakili Muluzi powakumbutsa za mlandu wawo wakatangale.

Padziwonetsero zomwe zidachitika lachinayi m’dziko muno, ochita ziwoneselowa adatenga ma uthenga wowakumbutsa a Muluzi pa zamulandu wakatangale wokwana K1.7 billion womwe ukadali ku bwalo la milandu.

Mauthenga ena, omwe ochita ziwoneselowa anatenga ndiwowadzudzula a Muluzi kuti asalese kuchita ziwonetsero zokakamiza mkulu wa bungwe loyendesa chinsakho la Malawi Electoral Commission (MEC) mayi Jane Ansa kutulula pansi udindo.

Kumayambiriro a sabatayi, a Muluzi adayitanitsa atsogoleri a mabungwe omwe akukonza ziwonetsero zokakamiza mayi Ansah kutula pansi udindo kunyumba kwao komwe mwazina amawapempha atsogoleri wa kusiya kuchita ziwonetsero m’dziko muno kwasabata imodzi.

A Muluzi akuwaganizira kuti anasakaza ndalama za boma pomwe iwo anali mtsogoleri wa dziko lino m’zaka zapakati pa 1994 kufikila 2004.

Mlandu wa katangale wa a Muluzi, watha zaka zoposa zisanu ukadali ku bwalo lamilandu, ndikutsatira kusapeza bwino kwa mtsogoleriyu yemwe wakhala akupita kuzipatala za m’mayiko ena kukalandila thandizo la makhwala.

Discover more from Malawi24

Subscribe now to keep reading and get access to the full archive.

Continue reading