Boma likweza mtengo wa pasipoti

Advertisement

Boma kudzera ku nthambi lowona za anthu olowa ndikutuluka m’dziko muno la Immigration latsimikiza kuti posachedwapa likweza mitengo ya ziphaso zoyendera.

Poyankhula ndi nyuzipepala ino mneneri wa bungweli a Joseph Chauwa anati mphekeserayi ndiyoona koma akudikira kuti nkhaniyi akaisiye kunyumba yamalamulo kuti aphungu akaikambilane ndipo ngati aphunguwa angavomereze, chiphasochi chikwera.

A Chauwa anati chatsitsa dzaye ndikaamba koti ndalama yadziko lino pakatipa yagwa mphavu zomwe zapangitsa kuti mitengo yazinthu ikwere komaso ati papita nthawi yaitali iwo chikwezereni mtengo wachiphasochi mumchaka cha 2009.

Mneneriyu wati boma likumasakaza ndalama zochuluka anthu akamapangitsa ziphaso zawo ponena kuti chiphaso chilichose boma limaikapo ndalama yosachepela K80,000 zomwe ati ndizokwera kwambiri.

Mkuluyu wati pakadali pano ngakhale sizinadziwike kuti mtengowu ukwera motani komaso ukwera liti, koma boma likufuna kuti aliyese azizipangira yekha chiphaso chake pofuna kuchepetsa ndalama zomwe boma likumaononga.

Izi zikutanthauza kuti boma siliziikaso ndalama iliyose munthu akamapangitsa chiphaso chake zomwe zingapangitse kuti mtengo wachiphasowu ukwere ndi ndalama yochuluka kwambiri.

“Ndizoonadi, ife tinafusidwa kuti tiunikeso mitengo yazinthu zimene timapeleka kwa anthu kuphatikizapo passport. Chachikulu chomwe chapangitsa mchakuti mtengo wapanowu ndiwotsika kwambiri poyelekeza ndi ndalama zomwe zimalowa kuti pasipoti iliyonse ituluke bwino bwino.

“Pamtengo wapanopawu boma likumalowetsa ndalama pafupifupi K80,000 pa passport imodzi nde chomwe tikufuna kuchita ndichoti munthu azingopeleka mtengo wa zonse zomwe zimalowa pa pasipoti zomwe zikutanthauza kuti zikatero boma siliziikaso ndalama iliyonse munthu akamapangigsa chiphaso chake,” anatero Chauwa.

Mkuluyu anati pakadali pano bungwe lawo likuunika bwino bwino zankhaniyi ndipo akamaliza kuunikaku ayitengera nkhaniyi Ku nyumba yamalamulo kuti aphungu akavomeleze kapena kutsutsa zakukwezaku.

Pakadali pano, mphekesera zosatsimikizika zikusonyeza kuti ngati aphungu anyumba ya malamulo angavomereze kukweza mtengowu, chiphaso chotchipa chichoka pa mtengo wa K48,500 ndikufika pa K80,000.

Advertisement

10 Comments

  1. Malawi, time of destruction has come devil is going to an advantage of our sicknesses, poverty and mistrust,kubamakoloathuwa and we’re going down, only change of power will take place but the of the people and our readers remain the same and it’s only GOD who will bring this to an end, may GOD judge on our favour (malawi) belongs to us.

  2. Guys let unite each other so that we can sorved what we can do to approve our to be strong ? like other countries not in that way even u MP’s there is no need to allow that because is already useless

  3. Even that spokes person is a Big FOOL!!how can you agree with that stupid issues ,you are a big fool he me very well YOU ARE A FOOLS WHO EAT YOUR OWN VOMIT LIKE A DOG ,And the one who send you all of you all you are FOLISH ,YOUR wizards,Ana a njoka inu

  4. Even that spokes person is a Big FOOL!!how can you agreed that stupid issues ,you are a big fool he me very well YOU ARE A FOOLS WHO EAT YOUR OWN VOMIT LIKE A DOG ,And the one who send you are all FOLISH ,YOUR A wizard

  5. It”s a bull shit to hike the price of passport in Malawi, look SA his price is times 3 already our price we got its R300 only do this this is your are to collect money from poor and enrich your self ?All of you you are fools from top up to the one at the migration, you are good for nothing pple, Salvages, Useless ,Trush, Rubbish, nicopump,babaric, Chief of fools

  6. Aphungu athu mukadzangovimeleza zimenezi musadzayelekeze kupangitsa misonkhano mumadera athu,
    Ndasiyira pomwepo

  7. Pa bingu pasipoti inali k15 500 koma apitala anakweza ndikufika k48 500 kuti amphawi azivutikabe poti zanu zikuyenda ndi kuba komwe ndi munthu waumphawi akafuna chiphaso aku immigration amafunaso ndalama zapadela kuti utenge chiphaso kkkkkkk mayo malawi mwagulisa abale anga .

Comments are closed.