Ambiri ali pambuyo pa Chilima, achina Obama ndi Kasaila kumeneko – watelo Ngalande

Advertisement
Peter Mutharika

Sizili bwinotu a President ndipo ena amene akumabwela pamaso panu ndi kumati ndi anu, musawamvele chifukwa usiku akumanka nakanyonyomala kwa wachiwiri wanu kukachongetsa.

A Lewis Ngalande amene ndi mkulu wa achinyamata muchipani cholamula cha DPP ati ngakhale gulu likuoneka ngati likukonda a Mutharika, pansi pa mtima anthuwa akufuna a Chilima.

Lewis Ngalande
Ngalande: Ambiri akufuna a Chilima.

Mu chikalata chimene atulutsa chopita kwa a Mutharika, a Ngalande auza a Mutharika kuti adzuke ndi kuyamba kukonza chipani tsopano.

A Ngalande ati zimene akuchita a Mutharika zongokhala ngati mu chipani chawo mulibe mavuto ndi zibwana chabe chifukwa kugawikana muchipani ichi kwafika patali.

Iwo aulula anthu ena amene nawo akuimila kumbuyo kwa a Chilima kuwafuna kuti nawo atenge chipani cha DPP pa ulendo wa 2019.

“Musayese ndi a Kaliati, a Ngumuya, a Kalindo ndi a Masangwi okha. Kuli gulu uku,” alemba choncho a Ngalande.

Mwa ena, iwo ati kuli a Peter Kumpalume, a Malison Ndau, a Aaron Sangala, a Grace Obama Chiumia ndinso a Francis Kasaila amene akufuna kuti a Chilima atenge boma.

Advertisement

13 Comments

  1. Masiku otsilizadi koma!! Mathews 24:33-36 maganizo anga chabe

  2. Chilima sangawine ndipo akagwere uko with his divide and rule.APM alamulanso ndipo chilima akanangolekelatu akuchitazi

  3. Apa pakufunika bwana mthalika apume kuti alandire ulemu coz DPP foundation yake inalikale yakugalukira ilindi demon imene ikuyenda ndi chipanichi, msaiwale malemu bingu anagalukira muluzi ndikuwatenga a joice banda, kenaka nawo a joice banda kugalukira bingu ndikuyamba pp ndi a khumbo kachali koma sanapitilire limozi ndikusiyanaso then a joice banda kulephera zisankho, apa amthalika ndi a chilima kugalukiranaso nchachidziwikire amthalika akakakamira nawo bwana chilima ayamba chawo chipani, Nyumba foundation ikapotoka zimatero, pempho amthalika akanakhala wina akanangopuma kuti azalandire ulemu wawo bt akapanda kutero mmmm kwaine sindikuona tsogolo lawo mzisankho za chaka chamawa, zikomo kwambiri.

  4. Apa nzongofunika a mthalika apume chifukwa zinthu sizilibwino, DPP inayamba ndi demon yogaluka ku UDF, kenaka nayo pp inazagalukako, apo nawo a khumbo kachali anazasiyanaso ndi a joice banda apa tikuonaso nawo a chilima akugalukaso kwa a mthalika nzosadabwitsa coz ndiye foundation ya DPP ndipo zichitika, nkofunika amthalika angopanga regsin kuti DPP mwina itha kukodzedwa kuchoka ku demon yakugalukilana ija zikomo kwambiri.

  5. Zoti chilima alamulira mzosakaikitsa wina afune asafune we will vote for him…… chilima woyeee

Comments are closed.