Ku nkhondo ya ku DPP, ana a mma Yunivesite ali mbali ya Mutharika

Advertisement
Peter mutharika

Nkhondo ija ya Absalom ndi Davite yavuta ku chipani cholamula cha DPP. Ndipo pamene aliyense akukokela mbali yake, nawo ana a mu sukulu za ukachenjede ati asatsalire.

Ana a mu sukulu za ukachenjede a chipani cha DPP auza Mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika kuti iwo akufuna a Mutharika ayimile chipani cha DPP mu 2019.

Peter mutharika
Ana a mu sukulu za ukachenjede a chipani cha DPP asankha a Mutharika.

Iwo anena izi pamene anakumana ndi a Mutharika ku Sanjika pa nthawi imene mu chipani cha DPP anthu ena akhala akufuna kuti a Mutharika atule pansi udindo kuti m’malo mwawo pabwele a Chilima amene akuti ndi wa chinyamata.

Koma polankhulapo pa nkhaniyi, atsogoleri a ana asukuluwa ananena kuti anthu onse ofuna kuti a Mutharika azisiye ndi anthu okhumudwa chabe.

Iwo anaonjezelapo kuti anthu onse a chipani cha DPP mtima wawo uli pa a Mutharika.

Polankhulapo a Mutharika anatsimikizila ana asukuluwo kuti iwo ayima 2019 pa tiketi ya DPP ndipo onse ofuna kuti iwo achoke alemba mmadzi.

 

Advertisement

4 Comments

  1. Muime musaime DPP out of the government 2019 alowemo anzanu inu mwaonjeza

  2. Iiiiiiiiii, koma abale pali ndalama-Eeeeeee, simanamadi . Tima k20 000 tomwe mwalandilati mpakana basi mwakopeka kugulitsa ufulu wanu wosankha yemwe mukufuna ?

  3. Munthu ukakura ndibwino kupuma kuti ulandire ulemu, mesa amati achinyamata ndi atsogoleri amawa? nanga mawa lizakwana liti ngati okalamba sakupeleka mpata? okusapotaniwo choonadi akuchidziwa koma akungofuna akudyeleniko kaye timakhobidi.

  4. Kuima sivuto bwana koma ngati kwalembedwa kuti inu simuzawina basi ndi wautali ku Ndata.

Comments are closed.