Tinanena kuti a Mutharika ndi lebwedelebwede, onani lero Callista wagwilizana nafe – Mia

Advertisement
sidik-mia-

Ati iwo adanena kale kuti dziko liri mmanja mwa agalu koma ena adali kukayika, tsopano pano ndi uthenga umene afuula Mayi Callista Mutharika mu chipululu kuti a Peter azitaye ndiye kuti zaphelezera basi.

Amene akutchulidwa kuti azakhala wachiwiri kwa a Chakwera pa chisankho cha 2019, a Sidik Mia ati kubwela poyera kwa Mayi Callista Mutharika ndi kunena kuti 2019 chipani cha DPP sichipambana ngati a Peter Mutharika ati ayimile ndi kugwilizana ndi zimene iwo ndi a Kongiresi akhala akukamba.

sidik-mia-
Mia: A Mutharika ndi lebwedelebwede.

Polemba pa tsamba lawo la pa Facebook, a Mia ati kubwela poyela kwa a Callista ndi kuchenjeza anthu a chipani cha DPP komanso kutonza utsogoleri wa alamu awo nndi umboni oti mu dziko muno zinthu sizili bwino.

“A Mutharika ndi lebwedelebwede, ndipo kulephera kwawo kukuchita kuonekelatu,” analemba choncho a Mia.

Mwa zina, a Mia anatchulapo nkhani ya maphunziro a ku Yunivesite ndi kudandaula kuti boma la a Mutharika likulephela kuwalongosola. Iwo anafunsa kuti: “kodi maphunziro tsopano asanduka a anthu a chuma okha basi?”

Iwonso anakambapo nkhani ya kusowa ntchito ndi ya kuchepa kwa malipiro a anthu ogwila ntchito boma, zinthu zimene akuti zikuonetsa kuti a Mutharika akuvutika kulongosola boma.

Advertisement

3 Comments

  1. Kanyimbi akugwirizana ndi zoti a Chilima azayimire DPP. Koma zoti malipilro m’boma akuchepa ndiye mmmmm ayi. Nkhani ndi yoti ogwira ntchito m’boma ambiri ndi a ulesi ndipo ndalama zomwe akulandira ndi zochuluka kwambiri poyerekeza ndi ntchito yomwe akugwira.

  2. MIA ndiwe wabodza. Lebwedelebwede umatanthauza Msowoya osati Mutharika. Usanamize anthu

Comments are closed.