A Mutharika akulingalila zonyonga onse okupha ma albino

Advertisement
Peter Mutharika

Wamisala anaona nkhondo. Ataopseza kuti ayenda buno bwamuswe pofuna kukakamiza boma la Malawi kuti lizinyonga anthu onse opezeka kuti apha albino, a Winiko akuoneka ngati tsopano atha kumvana Chichewa ndi Mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika.

Chikalata chimene atulutsa a ku nyumba ya boma chaonetsa kuti Mtsogoleri wa dziko lino tsopano akulingalila ngati zingakhale zothandiza kuti azinyonga anthu onse opezeka kuti apha munthu.

Peter Mutharika
a Mutharika akulingalila ngati zingakhale zothandiza kuti azinyonga anthu onse opezeka kuti apha munthu.

Chikalatachi chatulutsidwa pamene a Malawi atutumuka ndi kuphedwa kwa a Mcdonald Masambuka mu boma la Mangochi.

A Masambuka anali munthu wa chi albino ndipo anaphedwa ndi anthu amene amakhulupilila zopusa zoti mafupa a Bambo Masambuka angawalemeretse.

A Mutharika mu chikalatachi alonjeza kuti ngati boma iwo achita zotheka kuti anthu onse okhudzidwa ndi imfa ya a Masambuka abweletsedwe pa Khoti ndi kulandila chilango choyenela.

A Mutharika aonjezelaponso kuti anthu akufunika kukambilana moona mtima pa nkhani ya chilango chonyonga kwa anthu onse opanga chipongwe anthu a chialubino.

Advertisement