Iwalani zotenga boma a Kongeresi, anthu kummwera sakukudziwani ndi komwe – Mpinganjira

Advertisement
brown-mpinganjira

Wamasuka tsopano m’busa Brown Mpinganjira. Wayambapo zija zokhuthula mawu pa misonkhano yandale. Nkhani pano si ya PP anaisiya ija koma ya DPP. Ndipo iye wachenjeza anthu a kummwera kuti asazayese kuvotela Kongeresi.

Amene anali wachiwiri kwa President wa chipani chotsutsa cha PP a Brown Mpinganjira anenetsa kuti 2019, chipani cha DPP chikupitiliza kukhala m’boma.

brown-mpinganjira
Mpinganjira: Chipani cha DPP chiipitiliza kukhala m’boma.

Polankhula ku Phalombe kumene kunali msonkhano wa chipani, a Mpinganjira anenetsa kuti otsutsa a Kongeresi alibe kuthekela kochotsa DPP.

Iwo anati chipani cha MCP ndi cha anthu a tsankho ndipo atati apambane lero, iwo sangaganizile ndi komwe anthu a kummwera.

“Kuno ku Phalombe, MCP siyimikako munthu ndi komwe. Mukuti amenewa kupambana angakuganizileni ndi komwe, adziwa bwanji zokhumba zanu?” anatelo a Mpinganjira.

Pa msonkhano omwewo, a Mpinganjira analandila anthu oposa 400 amene amati achoka ku chipani chawo chakale cha PP.

Iwo anati PP tsopano yatha ndipo anthu asamakakamilebe ngalawa yomila ndi madzi ngati imeneyo.

 

Advertisement

One Comment

  1. Mmodzi mwa zitsiru zopanda phindu ndi Brown Wadyera Mpinganjira!Munthu wadyera wodzikonda!From UDF to Ubusa to PP to DPP!Useless a#*”shole!Ndawi yanu inapita baba!

Comments are closed.