Chitetezo chili pa nsalu ya DPP basi: mtsikana adulidwa ziwalo, wina aphedwa ku DPP

Advertisement
Chikwawa

Pa ngodya zitatu za chipani cholamula cha DPP chija, imodzi ndiye ikukhala ngati ikuvutilapo. Anthu akugonabe ndi mantha, Chitetezo ndi kumpanda wachifumu kokha basi.

Anthu a mmudzi mwa Goma m’boma la Chikhwawa akukhala mwa mantha zigawenga zitapha ndi kudula mutu komanso ziwalo zobisika za mwana wina wa mmudzimo.

ChikwawaA Polisi ati Mayi wa mwanayo anamusiya ndi m’bale wake pa tsikulo iwo ndi kupita kukasaka ziwala.

Mmbuyomu ati kunabwela zigawenga zomwe zinapha mwanayo ndi kumuba, izo zinamudula mutu ndi ziwalo zobisika. Kenako zinakamuponya pa sukulu ya mmudzimo.

Pamene ku Nkhatabay, Apolisi ali pa kalikiliki osaka zigawenga zimene zidapha Bambo Levi Phiri a mmudzi mwa Nyambwani, Mfumu Yaikulu Fukamapiri.

Malinga ndi Apolisi, a Bambo Phiri adasowa kwa miyezi itatu koma kenako anadzaoneka pa 27 mwezi watha wa February ali chiledzelere.

Ako kadali komaliza iwo kuoneka ali moyo, kenako anapezeka ataphedwa.

Advertisement

37 Comments

  1. olo boma lachipani chimodzi anthu akaphana basi ndiye lero mukunena chipani cha Dpp ngati ndichimene chikutuma anthu?zopusa eti.2019 DPP m’bomaaaaaaa

  2. olo boma lachipani chimodzi anthu akaphana basi ndiye lero mukunena chipani cha Dpp ngati ndichimene chikutuma anthu?zopusa eti.2019 DPP m’bomaaaaaaa

  3. Maganizo oputsa kwambiri, nanga ife tisiye kukhazikitsa chitetezo mudziko mwathu chifukwa choti ku maiko akunja anthu akuphanaso? Nanga ngati nkhani ndiyoti maiko onse anthu akuphana ndiye dpp siingakwanitse kukhazikitsa chitetezo kuno ku Malawi,nanga anaikiranji ngodya iyi yoti “chitetezo”? Or mkadzi kufunsa mwamuna wake ,nchifukwa chiyani ndalama zonse mwamwera mowa? Ndiye mwamuna amvekere anzangaso ku manyumba enawa amweranso mowa ndalama zonse.

  4. Is not about DPP!!! I think adim is little bit stupid coz kuphana is all over the world what about Nigeria?south africa? Rwanda? Maiko anenewo kuliso DPP?

    1. olo pamozambique pompano kuphana sinkhan tiziti kunonso tikulamulidwa nd dpp? tamalembaniko nkhan zopasa mudyo

    2. Uchitsilu ndikukula mopusa aMalawi timadana ndi munthu akudzudzula kapena akulankhula kolakwika kuti kakonzedwe. akazapangidwa chipongwe amanu ndipamene mutazapitilize kusangalala ndi kufaniza malawi ndi mozambique,south africa nigeria. kulankhula mopusa anthu pamene anthu akuvutika mMalawi . akazachotsedwa abambo anu chosambila muzasangalalebe ndi DPP yanuyo. ukakhala ku south africa chikhale choopsezela anthu? bwanji osakhala ku DPP komweko? chothawila Malawi kukakhala kwina pomwe DPP ikupanga zokusangalatsa mchani? mulungu akukhululukileni. simungamve nthumadzi ndikuphedwa kwa mMalawi mzanu zoona? kusangalala pamene mMalawi mzanu wadulidwa manja? Mulungu akutsekuleni makutu ndi maso kuti muzidziwa choipa ndi chabwino.

    3. #Ayao… Mukutipo chani apa nanu mukundiuza zophana kumalawi zayamba lero maboma onse apita aja zophana zinali mbweee was that Dpp kapena? Mukundiuza kuti ikachoka Dpp palibe azaphedwe, pokhala ngodya yachipani sizitanthauza tixakhala bata.

    4. Chalakwika ndi kutchulidwa dzina la DPP??? potidziwitsa nkhani imeneyi adakati bwanji tiyeni tikonze mwina tsiku lina tingadzakhale amzeru ophedwawo ali ambali yathu. dzindikilani kuti mwana wakhalidwe lonyansa amatukwanitsa makolo ake koma zonyansazo wapanga ndi mwanayo . osamakhala ndi ndi mkhanza mumtima kuti anthu asamatulutse chakukhosi. Komanso nthawi yoopa chithunzi idapita kale kale. Tsono munandilongosolele momveka mau amene adalembedwa pansalu yachipani chomwe chikulamula dziko lathu la Malawi. Tanthauzo la mau oti : CHITETEZO. pepani bwana sikudana ndi chipani chanucho ai. ndichanu chipanicho palibe angakulandeni bwana.

    5. Inu man mukuoneka kut muli ndi gulu lanu together with admin nkumapha anthu kuti muziti ndi DPP chifukwa chitetezo ndi imozi mwa ngodya yao ndakuonani

    6. Mulibe ndi zelu zomwe anthu inu mungamasekelere zoipa zuchitika mkuma ombera mmanja and mukupanga compare ndi maiko ena chifukwa chani mmagwiritsa ntchito malamulo awo ?ndinu zisilu supit zanu mwanva ?

    7. Kulibe chabwino kumalawi ndithu moti munthu wazelu zake angamasangalare pamene ena akuphedwa ?ndikumalankhula zopusa ngati zimenezi zisilu

    8. Hahahaha Lex you r the one stupid, palibe akusekelera apa koma tikudana ndi zotikwana chipani pa kuphedwa kwa anthu atatu dela kumeneko. Dxiko lonse lapansi uchifwamba wavuta even Super powers akulemphera kuthana nalo ndiye simungawele apa kumatukwana kuti uchifwamba uzathe I think boma lizalembe apolisi munthu aliyense wapolisi wake. Mind you wapolisi sangakhale malo alionse pali mmalawi. Tikudziwa mumadana ndi Dpp koma mukamapanga criticize muziona ndi zinthu zake.

    9. Iweso uti chani chani apa ndiwe kape iweyo ngakhale utati chani koma sindimasamala kuti ndi ndani kaya ali kuti koma ndiziyankhulabe pa zoipa zimene zikucitika iweyo uzikhala ndi chimwemwe ndikumasangalala pamene anthu akuphedwa koma ineyo ayiii!let me say that u r very supit together with the one who hav bin sent u to say dat floosh reply fulk u shit .

    10. Moti DPP iziopedwa kuposa 3 march mmene idalili??? manyazi mulibe ndithu ??? mwati akumatuma ndani ndi cholinga choyipitsa dzina la DPP????? Mwana DAUSI uja nanga???? Musamakhale ndikukula mopusa kamba koti ndinu olamula. mukufuna anthu azikhala ngati akhungu koma akuona zomwe zikuchitika???? Tiyeni tizithandizana kufotokoza pamene palakwika mwina tizakhala ndi Malawi osililika mtsogolo. Umoyo wa ulamuliro uli ngati katungwe, mmawa zinthu zimasintha mkuzalamulidwa ndi ena.

    11. @Issac Malinga you are welcome if you have an evidence to what you are talking about. Don’t measure and try the level of running water in the river with your leg.

    12. Hahaha LEX ukuonesa ukape wako onse apa ndiiwe, palibe chanzeru ungakambe apa, kuphana palibe angakukwanise unless zigawenga zizathe zomwe mzosatheka. Uzikapusitsa ma zoba osadziwa zimenezo. Watumidwa ndi amene walemba zopusazo Dpp , MCp or any party siingathese vuto lophana coz izizi akulephera maiko omwe ali ndi ovaya nde mukanene Malawi. Sindikusangalala kuphedwako koma zomalozana zala pankhani iyi ndikumbwambwana

    13. Koma kwayine chimene nudziwa chilichonse dziko athu amablema chipani cholamula apolisi adilikira amalamulidwa tsogoleri amene akulamuli pathawiyo chifukwa sitinga bleme CHAKWERA ndiye apapa ambiri akuwonetsa umburi DPP ndiyo imene ikulamulira

  5. DPP inapita ndi munthalika basi zasalazi ndi bamva basi Kodi kungakhale bwanji chitetedzo akupha anthu ali aboma omweo? tiyeni amalawi tidzigophepephela kwa mulungu azitipatsa chitetezo

  6. Zoona Kwambiri Chitetezo Kulibe Ndalama Zaboma Zikukhala Ngati Akuika Mumthumba Lobooka Kuti Chaponda, Goodle, Nakhumwa Ndi Ena Ambiri Azitola, Anthu Akuphedwa Ngati Nkhuku, Kugwililira Ndie Kwapita Patsogolo, Ndi Zina Zambiri. Ngakhale Kumpandakoso Chitetezo Kulibeso. Dzikoli Akuliteteza Yekha Mulungu Basi

    1. Vuto umangokhala mpheto mwa akazi uziyenda uzaona kuti bola Malawi go to south Africa, nigeria, Rwanda uzaziwa choona kuti vuto si DPP

Comments are closed.