Achenjezeni a Mutharika, JB akubwela kuzayima pa zisankho za 2019

Advertisement
Malawi Joyce Banda

A PP kodi mulipo? Pitani ku maofesi a chipani chanu chifukwa Mtsogoleri wanu ati akubwera ndipo 2019 akhala akupikisana nawo pa chisankho.

Malinga ndi malipoti a olemba nkhani, Mayi Banda alengeza zoti azapikisana nawo pa chisankho cha 2019 kudzela mwa mneneri wawo a Andekuche Chanthunya.

Malawi Joyce Banda
a Joyce Banda akubwera kumudzi.

Ngakhale a Banda anena zoti azapikisana nawo mu 2019, iwo sananene kuti afika mu dziko muno liti potengela kuti zipani zina zikuoneka kuti zayamba kale kampeni.

Padakali pano chipani chomwe adasiya Mayi Banda cha PP chasasuka ndipo ena mwa aphungu awo aoneka kuti akulowera ku chipani cholamula cha DPP.

Chigonjeleni pa chisankho cha 2014, Mayi Banda anachoka mu dziko muno ndipo mpaka pofika lero sanabweleko.

Mmbuyomu Mayi Banda akhala akulengeza kuti akubwera ndipo anthu akapita kokawalandila, iwo samabwela ndi komwe.

Advertisement

146 Comments

  1. MCP ndidiru ngakhale zitsilu zina za MBC zapanga program yoyipitsa mbili akuti Never again akunama ana achepa akumuwopa chakwela ife program yomanyoza munthu amene anamwalila sitisangalatsa kampeni satelo tiwonetsana 2019 ngati simupitaso Ku amelica kukakhala mukuluza

  2. KUVOTERA JB NDIYE AYI, BOLA CHAKWELA. She managed to dump her pp supporters and went on Diaspora osabwelanso, osalankhulananso ndi omusatila. Ndiye lero akibwera kuzawagunanso kuti amuvotere? Only fools can

  3. Joyce banda sangabwere nkudzaimanso pa ticket ya pp ngati mtsogoleri wao. Akuopa nkhani ija ya cash gate, ndipo akangoonekera basi zake zadalatu.

  4. JB ndi mbuzi ya munthu angawasiye anthu kuthawira kunja ndiye lero abwere kut anthu amuvotere. Ngati kuli Chitsilu cha mtsogoleri ndi JB. Ndi opusa amene atamuimbire m’manja Jezebel.

  5. Ibwere mbava yaikazi imeneyo inatidyera ndalama Ibwere ndithu tikudikira ,atipeza peter ndi owinawina kale

  6. Hon Lady deserted her own country, why coming now? Prof the incumbent wagwiratu mseu, zoti mumulanda mpando muiwale.The empty coffers he inherited are now full to the brim…..Tiwonetsana 2019.

  7. zopoira mukukangana apaz ine ngakhare ndili ochimwa ndikufuna ufumu wakumwamba ubwere 2019yi isanafike kut mwana wamunthu asalamulilenso kwakwana

    1. Masapota azipani Mupindula chani nokha nokha kumenyana mumenyerana zinthu zaweni ayini ake ndi olemela angoyenda thima lili zi

  8. same how be happy my poor friends its time to wear new clodes bcoz its the only thing our leaders can offer for us (Malawi)

  9. Bweran Mayi Maluz Kuno Nanga Sichithumba Cha Kwacha Munatenga Mwina Pano Chapanga Mature Munyumba Munatimangira Zija.

  10. mbavai amunthalika musadzaimange mudzandikile mudzaigwetse ndi voti pambuyo pake mudzamange ndimulandu wakatangale uja oba ndalama zathu zija

  11. Aaaaa kodi panangoutola iye mpandou angoti basi ,mama time is over, palibenso zoti muzaununkhanso mpando umeneu ,mpaka siku lakubwera chauta,

  12. Ambili amangidwa ena kuzipha chifukwa chaiwe pano Moti wasala ndiwe kuti ukayankhe mulandu uja wakutibela ndalama zanthu zijaya.Tikulandila koma osati ndi mtima osangalala.

  13. Ngati adalephela kuwina ali m’boma what more if she’s outside the government? Mumuwuze asavutike mkugawanso zina ng’ombe. Ife sitikumufuna. Ndiye lingakhale dziko lanji lolamulidwa ndimzimayi.

  14. We don’t need her, who is she? very very bad woman!!! ngati amkafuna kuzayimilanso amkathawilanji? kholo angathawe mkango m’nyumba muli ana ake?

  15. Kodi Mwayamba Kufuna Kuno Muzabeso Achisiru Inu Manyazi Mulibe Okuvotera Inu Ndiye Ndi Ana Anu Osati Anthu Amaganizo Ngati Ife Ukunama

  16. Kkkkkk…… Ndikachan Kameneko Kut DPP Itutumuke? Anali M’boma Koma Anakhala Postion 3,nde Angapange Chan Pano? Iye Azipanga Phada Wakeyo Ndi Lazalo!!!!!!!!

  17. zopanda chikhulupiriro chifukwa muli mau oti ‘ati joyce banda akubwera’ anthu akhala akumva zomwezo kanthawi.

  18. Waiting for her to arrested just soon voting time is far just to step in home land is already case kkkkkkkkkk

  19. Mayi wakuba ameneyu sabwela azafela komweko kuvotela wasiketi kubesa.kuwina ameneyu amuna onsee kumangidwa.

  20. Kkkkkk amayi tsopano takulandilani kunyumba koma musayembekezele kuti mumaka 2019 chifukwa dpp ipitiliza kulamula mwina mwabwela kuzasamutsa katundu otsala

  21. Hahahaha do u think angabweledi even atabwela only fools will vote for her. Munthu anatithawa uyu titamuvotela

    1. Kkkkk sanathawe man or akanakhala komweko palibe chomwe akanachita she is here in capetown south africa ndipo akubweladi dzaimilira inu mpeee

    2. Man hestings vuto amalawi sitimatha kutsata zithu Joice akanakhala kuti anaba anakamangidwa kale kale vuto timadana ndi chilungamo Joice Banda anaima pachulu ndikuuza mtundu wa amalawi anthu omwe ndikungwila nawo tchito akuba ndalama zaboma and anthu omwe anabawo anamangidwa tilitu ndi international criminal court anakatha kumumanga kale kale ubwino wake peter muthalika chilungamo chake akuchidziwa

  22. Dpp mukungoyiopa koma ngati jb angaime nde dpp iwonjezera mwai otsogolera a malawi beyond 2019. Personally i believe kuti ngati jb ayime mu 2019 nde kuti chakwera ayiwale zozalamulira malawi…therefore mama u r welcome kuno ndi kwanu zaimeni basi

  23. Kkkkkk! Which JB! The One Who Was Defeated In 2014 By The Same Mutharika? Oyenera Kuchenjera Ndi Wogonjayo!!!!

  24. JB is a threat to MCP not DPP! Reason; The North is pro PP! JB did not perfom well even in Zomba, her home district!

    1. They will be competing on position two….meaning there’s already no one there…m not supporting DPP…but if u can see the manifesto of opposition parties I don’t see them defeating the ruling party

  25. Ndiye amaiwa ndi abushili akhalale candidet ndiye ndani?? koma akafika sadzafikila mmanja mwa polibje?

Comments are closed.