Longezani muzipita ku Ndata – Mia auza a DPP

Advertisement
Sidik Mia

Ati kwawo kwatha. Ngati kuli kusolola, asolola basi ndipo amaliza. Tsopano ndi nthawi ya Kongeresi.

A Sidik Mia amene analowa chipani cha Kongeresi auza anthu a DPP kuti alongeze katundu wawo mmboma chifukwa 2019 kulibe kubwelelamo.

A Mia amene akuyembekezeka kuzakhala wachiwiri wa a Chakwera pa chisankho cha 2019 ati Kongeresi itenga boma basi.

Sidik Mia
Mia: Boma la a Mutharika lalephera.

A Mia ati a Chakwera ndiwo akhale Mtsogoleri wa dziko lino kuyambila 2019 ndipo achita zitukuko zodula mutu.

Iwo anadzudzula boma la DPP ati kamba kolephera kutukula dziko lino mu zaka zinayi zomwe akhala pa udindo ndipo m’malo mwake ayamba kujijilika pano kuyala miyala ya maziko.

“Pa zaka zinayi alephera kupeleka mwayi wa ntchito ku achinyamata, alephera kutukula dziko lino ndiye lero akati tiwavotelenso? Akunama,” anatelo a Mia.

A Mia ananena kuti boma la Mutharika tsopano likuyenela kulongeza katundu wawo ndikuyamba ulendo osamuka mmboma.

Advertisement

160 Comments

  1. Eya Mia sakunama za Dpp ndi mbava zaba ndalama zamalawi osauka m’kumagawana ma k40 million pamene m’malawi wosauka wakumudzi akuvutika ndumphawi wadzaoneni wina am’vekele koma Dpp udzikondabasi zachambabasi pamene mankhwala nzipatala mulibe anthu ambiri tidakamwalira padakapanda ma private clinic piter atsanzike watibela mokwana.

  2. Uyu alibe mbali Ali ngati hule mu ndale so anthu a nyakula mwatengeka naye mwayesa akuolotsani river Jordan eeissh mavuto alipo.

  3. ndalama ndi umunthu zonse zayenera kwamunthu kma mphatso ya utsogoleri ndiyakwamulungo 2019 tiligu mmatumba,namsongole kumoto¥¥¥¥¥¥¥¥¥¥

  4. in politics,people May become famous and second they become foolish people and finally they in devil peace ✌.only following Jesus is the best way so we can emulate Dpp,mcp or other parties but we are nothing to them so we should follow where we are going coz we don’t know a good leader but we should mulling over something when we shall voting in 2019

  5. aaah amia asaxipusiE makaladi tuwaziwa ife palibe game amasewela osaikapo juga azavoteledwa ndi asena nda chewa ananjoya nthawi ya gogo wankhaza uja

  6. DZUKA MALAWI DZUKA……….ANTHU MUMENE MUKUVUTIKIRA KUMALAWIKO BASI MUDAKALI KUSAPOTA DPP????? OOOOO SHAME ON YOU PLZZZ………WINA WACHITA KULEMBA KUTI DPP YIZALAMULIRA MUPAKA 1000 YEARS …….MWINA YIZALAMULIRA AGOGO AKO STUPID!!!!

  7. Pandale aliyese amayakhula zimene aķuona kut angathe kutero chocho amia anena mbali yao kuti awina ndio ndiye nao a dpp akut nafe tiwinaso ndie inu o komenta zikumaoneka kut aliyese akukokera mbali yake apa koma sinu andale mumangovota osewa anal chipani chimozi achita kumasitha ndie tieni tidikire 90mins

  8. Mia chilimikani kwambili tili mmbuyomo 2019 MCP boma basi enawa apite akalime ku ndata.Abe anthu ma alubino akhale ndimntendele paumoyo wawo

  9. Dpp or zinthu zitavuta maka singawine, oziwa ndale amawelengela,NOTE DPP IZAWINA KU THYOLO NDI MULANJE PANG’ONO BASI.you will mark my words.

  10. This z wat we call old school politics…dissing each other cant helf .Mr Mia just tell wat u will to wen u takeover the goverment…

  11. Kodi nkhaza munkapanga zija mukuganiza ngati anthu anaiwala? Nchipani chiti chimene chinkawaponya anthu mu ziwe la Ng’ona…#MCP. Nchipani chiti chimene chinkawqkhazika azimayi oyembekezera panseu chifukwa chopanda Card? #MCP. Nchipani chiti chimene chinkamenya anthu ndikuwqchita nkhaza popanda chifukwa? #MCP. Ndie mukuganiza kuti munthu wanzeru zake oganiza waumunthu akavotere MCP. ZIPHYERA za Mabala omwe Munawazunzira anthu Sizinafufutike zikadali mumitima mwawo. Akakumbukira AMADA NAWO KUKHOSI ULAMULIRO WANU WA MCP .

  12. Kodi nkhaza munkapanga zija mukuganiza ngati anthu anaiwala? Nchipani chiti chimene chinkawaponya anthu mu ziwe la Ng’ona…#MCP. Nchipani chiti chimene chinkawqkhazika azimayi oyembekezera panseu chifukwa chopanda Card? #MCP. Nchipani chiti chimene chinkamenya anthu ndikuwqchita nkhaza popanda chifukwa? #MCP. Ndie mukuganiza kuti munthu wanzeru zake oganiza waumunthu akavotere MCP. ZIPHYERA za Mabala omwe Munawazunzira anthu Sizinafufutike zikadali mumitima mwawo. Akakumbukira AMADA NAWO KUKHOSI ULAMULIRO WANU WA MCP

    1. Eeeti alibe manyazi chani wachake ndi wachake basi akuganiza kuti zomwe ankachita kale aleka??mesa it waz written and alinazo dongosolo lonse yoyendesera chipani akunama man kungowina adzayambiranso zawo zija.

  13. Hahahahahahahaha chipani chake chitinso choti uzikaima pagulu makolo anthu anavutika ife sitifuna kuona zomwe anaona makolo kkkkkkk

  14. Mmmmm I Doubt. U Cant Just Defeat This Mighty DPP on a silver plater. they are all over the country unlike MCP. Lets Wait And See Mwina Mia Waiwelenga DPP Which in real sense i doubt.

  15. Malawi Congress Party again? Mmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmnmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmmm ‘yalakwatu pamenepa’ Nkhuku zanga zapita basì!

  16. wakufa sadziwika, tiyeni tingodikira pang’ono. Kusankha ndi anthu omwe sadalankhewa ndi amene adzaika pa mpando munthu yemwe akufuna!.

  17. We take some of these empty sentiments as kicks of a dying Buffalo. MCP is a big threat and you may already having sleepless nights. Remember in the last election DPP and MCP were neck to neck. What more this time when DPP has lost penetration power especially in the central. You have to understand that this is the toughest campaign for DPP.

    1. Nanunso ambiri sanavote timkangoti dpp wawina maka ku lilongwe city chiwoko anthu wolembetsa analipo 4000 wovota 459 nde muona ulendo uyu tikavota

  18. Ndani munthu wamzeru angavotere MCP? MCP singawine 2019 zivute zitani, DDP ikhala ikulamulilabe up to next 1000 years.

    1. Hapana Chisingapere oyimba waku Zimbabwe anayimba choncho meaning PALIBE CHOSATHA ndipo DPP mukuiti izalamula mpaka mpaka ZOSATHEKA ZIMENEZO ndipo muzaona ngati kutulo DPP iri kunja kwa boma….

    2. Believe you me, mufune musafune DPP ikhala ikulamula up to next 1000 years. MCP sidzawinapo presidential elections.

  19. Hon.Mia Behaviour is like of himself.Kuchipembedzo matama ake ndiomwewo.Amafuta atakhala Mtumiki Muhamad zimangovuta.Wanena bwino kuti abweretsa chitukuko chodula mutu.Muyambenso kutidula mitu
    Mia kumbuka za Patel kwa Bvumbwe anawona zokoma chifukwa cholimbana ndi Boma.Mbuzi ndi ng’ombe zako zitha.Uyenda pansi.Umatsogolera kutukwana MCP lero ukufuna kutisikonezera chipani chathu.Ife sitinasinthe chipani.Koma iwe ukukhala ngati galu wachiwewe.Mpando ukufunawo ndi wa Msowoya ;Munthu wophunzila bwino ….aaaaa Mkaladi alamulile dziko la anthu akuda.Abakana ANgwazi zimenezo.Ife ayi .

  20. Kodi apapa sipoopsezelana ai aliyese akuyenera kulankhula kodi mukati ndiokuba ndiye wabwino osabawo alikuti? mu dpp chaponda bwaa wabwino tiyambe kuwachula apapa aaaa inu anthutu akuona inutu mudikile kaye muone kuti kumwera kutuluka chani? come 2019

  21. Ambuye tiomboleni awaso akuti yakwana thawi yawo yosolora tithawila kuti amalawi amzanga timaona ngati aziti thawi yobwezelexa ndalama mchimake koma kkkkkkkkkkkk mia ndiwakubadi eti

  22. ovota ali phe!! pano tisanamizane nkhani zili paliponse ndiza Mcp,ikuwina basi ndiye apa tiyeni tizingochezapo ngatinso timavota nawo

  23. Kikikiki! Asosola eti? Musandiseketse inu ndithu. Koma ali m’mavuto a chipani cholamulira no wonder they want to make a coalition with the other party

  24. Amia uzani mtundu wa amalawi zimene mudzachite mukadzalowa m’boma 2019 kuposa zomwe zilipo panopa.Amalawi panopa anachenjera kotero simungawapusitseso ndi kumawatuma kuti kandipheren brown mpinganjira ndikupatsan 5pin aliyese kulibe.Musasiye mlomo

  25. foolish government of muthalika tawonani 3440 000 000 000 zimene adalonjeza kuti apatsa amene akane electoral reforms beaure ndipo zadziwika tsopano misonkho yamalawi kuchitanayo zovetsa chisoni malawi akupita kuti?mmalo mopanga chitukuko ndalama mkumapatsa zidzete zama mp kuti zizikana ma bill chimenechi ndicho chazelu adapanga amuthalika ?Atule pasi udindo uku ndikupha dziko, supit zanu fulken u muthalika.

  26. A mia wakutumaniyo akupweteketsani chifukwa yemweyo 2014 adagwa chagada. Kodi mukatchalenja a Msowoya za u vice president mukuona ngat ndi mungatchalenjenso a president adziko lino? Mmm musamatero a Mia ine changa ndichisoni kwainu

    1. MAN TANG’ANANI KUCHIPANI CHOLAMULACHO NGATI KULIBE WAMAGAZI MMMANJA ? AND ONSE AMENE ANALI MAMAFIA NTHAWI YA MCP NDI AMENE ALI KU DPP NDIYE MUKT CHAN

    2. Munthu akafera ku Police Mbiri imaipa ndiya Police Yonse ngakhale individule Yemwe adapha Munthuyo atachoka ndikukayamba uphuzitsi

  27. Atsogoleriwo ali bho koma vuto ndi chipani chomwe akwelacho mkovuta kuwina “kongelesi( mcp) musandikumbuse kale ndalila”

  28. Mia galu wa ciwewe ngati iwe angakumvere ndani hule ungofuna mpando uyambe kaye wayang’ana ku mtundu kwanu ngati kuli wanzeru osamakangodya athese bwanji wayesa APM Nidi nzako eti ndipo ameneyu abwenze Cold storage ija galu wakuba uyu nadyanzi sukuona chitukukochi . Uli minister wa tranport unapanga cani iwe manyazi ulibe masaize ako ndife wamva

    1. Keneth Jere, why commenting ngati Sidik Mia amalankhula za kunyumba kwanu? Its people like you who destroys the good history of the party.

  29. CHITINI CHOPANDA MADZI PHOKOSO KWAMBILI, MIA KAVUWE VUWE KAYA CHAMBA CHIKUMUPWETEKA. ALONGEDZE NDANI NDIMAYESA IYE NDIYEMWE ANALONGEDZA DYELA. OVOTATU ALIPHEEE KUDIKILA TSIKULO DPP KUMABWELELASO M’BOMA.

  30. Awuzeni ayamba kulambula misewu poti awona kuti akungoluza zisankha zazing’ono zikachitika Dpp kwawo kwatha awa yanga ndi mcp basi

  31. ine ndimakonda MCP koma singachite Ku votera Mia or chakwera , better Peter yemweyu. the demon u know is better than the angel u don’t know

  32. Hahaha chipani chilichonse anachikhalapo …..kufuna ndiwo zabwino demet zako akuvotera a gonthi omwewo ine ndakukanira zopepera zakozo

  33. vuto lonyoza achinyamata ndilimenelo mr ibu lelo akuti mupakile. kumawapaka penti achinyata mwati ndi tsogolo lawo lelo alusa ati mupakile pepa mr.

  34. Mr Mia chenjerani ndi mayankhulidwe anuwo tsiku lina muzachita manyazi kwambiri, ndipo chomwe mungadziwe inu nachi ;zandalezi ziri ngati gemu ya mpira ndipo zidzimaziwika bwino lomwe ai m’mangoona zitatha basi. Choncho wopakira kapena wolowa sadziwikanso ai tiyeni tiyang’ane za kutsogolo kwathu kuti chingatipatse mulungu m’chiani DDP kapena MCP.

    1. the story is not about ntaba. and sinanene kut kwinako ndiabwino….am not either talking mcp or dpp. iam talking abot mia

    1. Udzakhumudwa ndipo sudzadya nsima azakoso ku zambia ankatelo koma mmene adagonjela Lupia Bwezani Banda wachipani cholamula mmmm zovetsa chisoni kunoso zichitika zimenezo

Comments are closed.