Musaope, gumulani nyumba zonse zomangidwa mu phiri – Khoti liuza a khonsolo ya Blantyre
Bwalo lalikulu la Milandu tsopano lamasula khonsolo ya mzinda wa Blantyre kuti ndi yololedwa kugwetsa nyumba zonse zomwe zamangidwa mu phiri.
Khonsolo ya mu mzinda wa Blantyre inauza anthu onse omanga nyumba mu phiri kuti asamuke. Koma anthu aja m’malo mosamuka anapita ku Khoti kukatenga chiletso.

Kwa zaka zisanu, a khonsolo akhala asakuchita kanthu ati kamba ka chiletsocho. Koma tsopano chiletso chija chachotsedwa.
Ndipo tsopano a khonsolo apeleka chenjezo kwa anthu amene akukhala mu mapiri a Soche, Ndirande kudzanso Mpingwe kuti asamuke ndi kugwetsa nyumba zawo.
“Ali ndi masiku 60 anthu amenewa, miyezi iwiri yeniyeni. Ikatha tikubwela tokha ndi galimoto zathu kuzasalaza,” anatelo mneneri wa Khonsolo a Anthony Kasunda.
A Kasunda ananenanso kuti a khonsolo apeleka malo kwa anthu 65 amene asamuke.
Iwo anati pamene nkhaniyi imayamba, anali ma banja 65 okha amene amakhala ku phiri.
“Tsopano alipo 300, koma enawo anabwela akudziwa kuti malowa ndi osaloledwa kukhala,” iwo anatelo.
69 thoughts on “Musaope, gumulani nyumba zonse zomangidwa mu phiri – Khoti liuza a khonsolo ya Blantyre”
Comments are closed.

Zagumulidwa kangati nyumbs zimenezi?
Nde nyumba zithatu btz popeza nyumba zambili zili mmapili pafupifupi location ina iliyonse
Kkkkkkkkkk
amkot alozesa azawo ogumula enawa ndi amfit
Kubwezelesa chitukuko mmbuyo bwanji munthu wamanga nyumba yake inu nde mugumuleso? Tamayendani a Malawi muziona mmayiko anzathu nyumba dzao kuti zili kuti pamwamba penipeni pa phili boma ndikwasatilaso komweko ndinseu opambana kwambili koma kumalawi iiiiiii mmmmh
Kazisasuleni bc azaona ngati boma ndilopweka
kodi boma limangoonelela mmene nyumba zimamangidwa,nanga malo amapereka ndani? osamalowetsa ndale. ndindalamatu kumanga nyumba.
Agumulidwe basi
Zaulendo uno
Malo ake omwewa a Chauta Namalengawa mukuti ndi a inu a boma?Ayi zikomo mukhale ndi moyo opanda malire inu ndi anzeru anuwo oweruza mosaopa Mulungunu.
Komaso boma apeleka warning kangati amwenyeso mugwetse apo ayi timenyanq
Amenewo achoke sioyamba kugumulilidwa nyumba mukafunse anzanu ku Bangwe.