Pulofeti amangidwa kamba ka ulosi wa bodza

Advertisement
Machinga

Tsopano mukakhala mmaluzi ndi kuganiza zoyamba bizimisi ya Tchalitchi muli muzichita uneneri, musamale. Azikumangani.

A Polisi ku Thyolo anjata ndi kutengela ku Khoti Bambo Sampulo Newiri a utumiki otchedwa Thamanda ati kamba kofalitsa uthenga wa bodza ndi osokoneza anthu.

MachingaMalinga ndi a Polisi, Bambo Newiri amene ali ndi zaka 40 akumachita utumiki wawo ku Thyolo umene ukupomboneza anthu.

Mwa zina, a Newiri amauza anthu owatsatila kuti asamatumize ana awo ku sukulu ndinso kuti akadwala asapite ku chipatala.

A Newiri anauzanso owatsatila kuti asalime minda yawo chaka chatha ati chifukwa Ambuye anawaonetsa kuti mvula siyigwa konse. Anthu anamvela ndipo ngakhale Mvula inabwela, iwo anali manja pindike. Owatsatilawo ati tsopano akukhalila kupempha kwa anthu.

Anthu a ku Thyolo ndiwo adakamang’ala ku Polisi kuti ziphunzitso ndi uneneri wa a Newiri ukusokoneza chitukuko ku dera lawo. Apolisi anapita ndi kunjata a Newiri. Ndipo adawatengela ku bwalo la Milandu.

Pa bwalo la Milandu, a Newiri aukana mlandu ofuna kudzetsa chisokonezo ndi zokamba zawo. Apolisi anapempha a bwalo kuti awalole kubweletsa mboni. Ndipo a bwalo anena kuti mboni zitatu zibwele pa 22 mwezi uno.

Otsatila a Newiri amene anawatsatila ku Khoti atavala zovala zoyela zokhazokha ananena kuti milandu yomwe akuzengedwa Mtsogoleri wawo ndi ntchito za Satana.

Advertisement

29 Comments

  1. Zisakhaledi kuti mwsona ndiosauka. Ena anatii abwezeretsa magetsi in 24 hours nakanika ataloledwa mwaatani?

  2. Mwina poti ndi prophet wosauka…. how many prophets and politicians including the president himself lie to us?
    Malawi too much bias that’s why they’re fighting with chavula……
    #ShitMind

  3. Kkkkkkkk koma utumiki winayu mmmm ayi bodza anthu tisawanamize, Kodi mesa Bible limanenetsa kuti udzadya thukuta lako? Komanso osagwila ntchito asadye? Ndiye iyeyu kuwauza anthu kuti asalime amati anthuwo azidya chani? Ndipo tsamba lake ndilitilo mu Bible limene limaletsa munthu kuphunzila? Kkkkkk koma yaah!! Komano kenako simulamula kuti akazi onse amene amabwela Ku utumiki wanuwo akhale anu? Mmmm musanyozetse dzina LA MULUNGU chifukwa chongofuna kutchuka mulangidwa nazo

  4. eeee ma prophets awonjeza aliyesetu.ndiye akhalatu prophet tiyeni amalawi tizilimbikira kugwira ntchito osati kunja kuchaka ndiye kuganiza ma plan owawuza anthu kuti mulungu wakulotesani kuti ndinu mulosi. aaaaa boma likamakulangani ndiye muziti loipa ayi mwaonjeza azilosi onyenga inu.

  5. Mpulofiti Wamulungu Sanganane Koma Wa Satan Amavuma Kanthawi Kochepa Kenako Mankhwala Akatha Ntchito Amangonena Zamutu Mwake Like What You C Let God Dell With Those Pipo Akumva Kuwawa Ndi Yesu Chifukwa Amanimizira Dzina Lake

  6. Mpulofiti Wamulungu Sanganane Koma Wa Satan Amavuma Kanthawi Kochepa Kenako Mankhwala Akatha Ntchito Amangonena Zamutu Mwake Like What You C Let God Dell With Those Pipo Akumva Kuwawa Ndi Yesu Chifukwa Amanimizira Dzina Lake

  7. Kodi Kumanga Opemphera Ndipomveka Nanga Kodi Okuba Ndarama Za A malaw Zogura Maize Wa Ziripati Ine Anthu Akuba Ngati Amewa Kungomupeza Gawo Lachuma Chakechose Alangidwe Komaso Zaka 50 Akugwirira Boma Ulere Chopusakwakeko Kuba God Adzaranga Mbara Zonse Kaya Kumudzi Kaya Ziri M.boma Zonse Adzaranga

  8. Ndi matsiku otsiliza ano kunalembedwa kale kuti kudzazuka aneneri ambiri onyenga ndendiamenewo msawaweruze azakaweluzidwa ndi Mwini wache

  9. Chabwino tamva komansotu kuli ma members of parliament and the president amalonjeza zoti sadzkwanitsa kodi kumeneku sikuyambitsanso business yobela anthu titani amenewa tsopano?

  10. eeeeee koma nawoso a police dzulo amafunafuna atamanga Mwiza chavula chifukwa chinyimbo yake den lero amumanga m’pulofeti⛪……..timva mawa kuti amanga owulutsa zanyengo⛅ poti nawoso amanama kwambilii……chosecho obaa chimanga komaso acashgate alipheee kunjoya ndidziko

Comments are closed.