Ine ndi kamnyamata kachisodzela – watelo Mutharika

Advertisement
Mutharika

Wakalamba wafuna. Mstogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika amene akhale ndi zaka 81 pofika 2019 ati iwo ndi kamnyamata kachisodzela ndipo azapikisana nawo pa chisankho mu 2019.

A Mutharika anena izi mu mzinda wa Mzuzu pamene anayima kuti apelike moni kwa anthu ena mu mzindawo.

Iwo anati mu chisankho cha 2019, apikisana nawo ngakhale kuti azakhale adakali agogo.

Mutharika
Mutharika: Wakalamba wafuna

“Anthu masikwano akukonda kukamba nkhani ya achinyamata. Ndiye upeza anthu a zaka 50, kapena 60, ngakhalae 70 imene kuzitchula kuti ndi achinyamata. Inensotu ndi wachinyamata, ndipo 2019 ndilipo ndithu, kuzathamanga nawo kuti mwina ndipambane chisankho,” anatelo a Mutharika.

A Mutharika anati chifukwa mayiko a ku Ulaya anawasankha kuti ndiwo otsogolera achinyamata mu Africa muno, iwo ndiye kuti ndi wachinyamata basi.

Zokamba za a Mutharika zachititsa jenkha a Malawi ena amene amayesa kuti a Mutharika atha kusiyila mpando kwa wachiwiri wawo a Saulos Chilima amene ali achichepele.

Zinamvekanso kuti a Mutharika akuganiza zosankha bambo George Chaponda kuti azatenge udindo wawo iwo akapuma koma a Chaponda atakhudzidwa ndi nkhani ya kuba chimanga, zinakhala ngati zasolobana.

Anthu ena ankanenanso kuti a Mutharika akuganiza zosankha a Ben Phiri kuti apitilize udindo wawo mu 2019 umu.

Advertisement

162 Comments

  1. Kkkkk kamnyamatadi eeeee not yet developed in his mind kkkkk .no wonder he tell lie after lie after lie.anyamata kunama is their habit

  2. A Malawi 24 ndinu zitsiru ndithu imeneyi ndi nkhani yoti mungatiwuze ife a Malawi itithandiza chiyani ifeyo ngati mumadana ndi a president nde ndinu opusadi ife tizipanga Debate nkhani yopanda nzeru ngati imeneyi? inuyo kumeneko muli ndi zaka zingati! stupit!

  3. Amene akuchemelela mkulu uyu ndi zitsilu komaso kut mufufuze ndi mbava zili mu office ku commenta za uchitsiru analowa mu office chifukwa cha chinyengo.

  4. mmmmm, mmmhuu amalawi zalakwika pati zomwe zanena mkuluyu, aliyense ali, ndi ufulu oyankhula m’ene iye akuzionela palibe chifukwa choti tikamuthele mau, kunena za chipongwe zili zonse anthu ambili mwalankhula za mwano komabe chomwe mungaziwe ndi mtsogoleli wanube basi. aaaa tiyeni tizikondana. inu nthawi zina tikamalankhula za mwano kunyoza, tisanayambe tizikhala pheeeee, mkumati kodi tsiku langa limati mumakwana ndi makonzeka mkupita kukapemphela cholinga Changa ndi chani? 1 tizaone za chikondi 2 ulemu 3 kulemekeza 4 kupilila 5 chiyambi cha mnzelu mkuopa mulungu pa zonsezi titaziganiza tisanamuyankhulile mnzathu zoipa ndi kunyoza titaganiza bwino mkuona kupelewela kwathu mwina sitingamatere tiyeni tisiye kunyozana wina akanena ndiufulu wake oyankhula m’ene mulili inu, tisangoti poti ndi mtsogoleli koma nayeni aiiii

  5. Munthu pala wawelera kuwaniche mahara yakuchepa, chikulongola kuti mudala uyu mumulomo mino alije kweni waluwa kuti wana chipala mmulomo

  6. Sakunama munthu akamakalamba amasanduka mwana. Kungoti mwana wakeyu mwano too much even ma advisors ake akungomuyang’ana kuti nyanga ya nsatsi izamufotele yekha.

  7. mukamanena zamtsogoleli musamaphatikize ndizamtundu ndizigawo musokoneza chifukwatu chitsulu chamisala chandala chopanda ndalama chilindimwini

  8. Ndiyengati ndikamnyamata kachisodzela,ife tikufuna munthu okhwima mzeru ndi odziwamavuto osati kamwana ayi kaona zambiri zikumuvuta.Anyamata azikhala ma khansara ndi ma mp nangaonse akakhala ana aziuzana nzeru zotani?

  9. Kamnyamata kopanda Mano aise tamuuze peteryo andopheze kumbayani kuli tansikana ta std 7 tikachinde paja peter anazolowela kubunyula uzazipwetekatu

  10. Wachisodzela ndi choncho thinking capacity imakhala low l see ,thats why malawians we are panic in any way round for more ask the journalist now

  11. Ichi ndichizindikilo choti amuthalika ndabidza ngakhale akuti kuwanenakuti ndabodza mkulakwa ,munthu wanzelu sangati ndimnyamata pomwe ali ndi zaka 79,kuwavotera mu 2019 mchimodzimodzi kumanga nyumba pamchenga mvula ikabwera imadzangoikokolora,…vuma wakara sekuru….

    1. Kkkkkkk koma ndiye azungu amavutikatu komwe uliko wth ur useless English , apa takuziwa kale unasiya xul nikuthawila ku #South_Africa

    2. Kungomukoza ..abale munthu z2 uyu..kut nxt tym.asadzalakwitseso..madziwaso.kulemba ndikuyakhula.zosiyana..koma i blve kut tonse tamuva zomwe amafuna kunena..so.plz kukozana ndikwabwino

    3. muphunzitseni pamene walakwisapo

      mukumunena ndiyeee adziwa bwanji???

      ku RSA kulibe zosekanaziiiii taaaaaa

      ndiku malawi Konka dziko loose lapansi umanenedwa ukalakwisaaaa chingelezi

  12. Indedi that’s an ironically I am speech osamaiwala paja munthu ukakalamba umakhala ngat mwana wakhanda ongokhalira kuyamwa… Kk I think he is just getting so exhausted by his position end perhaps pompano we would hear that he want to resign stepping down udindo wake

  13. Zikubwera mochedwa kusirira atakhala mnyamata, pepani Bambo vomerezani kuti ndinu Agogo, dziko lakukanikani kulamula, iwalani zoti mudzawinaso Agogo

  14. Madala ndinu agogo mbuya but our constitution does not bar you to take part. And we want even you as DPP to compete in primaries not imposing. I see young guys in the party with calibre like Getrude Munthalika, Ben Phiri, Chilima, Nankhumwa, Mgeme, Don Kalindo etc

  15. wakula ngakhale malamulo athu palibe Edge limit makamaka ’35’ and above inde kuima adzaima koma sadzapambana 1.old edge 2.wataya moralo on the ground e.g ma blackout,electro reform bill,pointing of top govt officials ,tribalism etc…

  16. Kkkkkkkkkkkkkkk nde choncho angasiye moyo wozikundikira??? Ngati munthu yekha akukanika kuzindikira kuti wakalamba do you think angakuthandizeni achinyamata. Watch out!!!!!

  17. Museum material. Akumavala thewela akuluwa. He’s 108 years old. Akachotsela zimene amadwala 87. 2019 paulendo. Chakwera ndinyamuleee!!! Bwampini watilephela!! (Singing).

  18. HAHAHAHAHA Wakoma mpando ongowukakamira mchifukwa chake adalowa usiku anthu akugona chonsecho palibe chomwe angaloze chamzeru chomwe apanga ndi k2000.00 komaso k5000.00 kuti amalawi adziwe zoti munthuyu ndi professor weni weni

  19. Zitsilu zizake zipezeka pompa zochepa mzelu kumati bwana bwana akhala bwanji bwana pamene ntchito mugwila koma malipilo sakupatsani nenani kt mbava musaope

Comments are closed.